Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yobu 1:9 - Buku Lopatulika

9 Nayankha Satana, nati kwa Yehova, Kodi Yobu aopa Mulungu pachabe?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

9 Nayankha Satana, nati kwa Yehova, Kodi Yobu aopa Mulungu pachabe?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

9 Satana adafunsa Chauta kuti, “Kani mwayesa Yobe uja amangokumverani pachabe?

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

9 Satana anayankha kuti, “Kodi Yobu amaopa Mulungu popanda chifukwa?”

Onani mutuwo Koperani




Yobu 1:9
9 Mawu Ofanana  

Kodi simunamtchinge iye ndi nyumba yake, ndi zake zonse, pomzinga ponse? Ntchito ya manja ake mwaidalitsa, ndi zoweta zake zachuluka m'dziko.


nati, Ndinatuluka m'mimba ya mai wanga wamaliseche, wamaliseche ndidzamukanso; Yehova anapatsa, Yehova watenga, lidalitsike dzina la Yehova.


Koma ananena naye, Ulankhula monga amalankhula akazi opusa. Ha! Tidzalandira zokoma kwa Mulungu kodi, osalandiranso zoipa? Pa ichi chonse Yobu sanachimwe ndi milomo yake.


Mwenzi atakhala wina mwa inu wakutseka pamakomo, kuti musasonkhe moto chabe paguwa langa la nsembe! Sindikondwera nanu, ati Yehova wa makamu, ndipo sindidzalandira chopereka m'dzanja lanu.


Pakuti munthu adzapindulanji, akalandira dziko lonse, nataya moyo wake? Kapena munthu adzaperekanji chosintha ndi moyo wake?


pakuti chizolowezi cha thupi chipindula pang'ono, koma chipembedzo chipindula zonse, popeza chikhala nalo lonjezano la kumoyo uno, ndi la moyo ulinkudza.


Koma chipembedzo pamodzi ndi kudekha chipindulitsa kwakukulu;


Ndipo chinaponyedwa pansi chinjoka chachikulu, njoka yokalambayo, iye wotchedwa mdierekezi ndi Satana, wonyenga wa dziko lonse; chinaponyedwa pansi kudziko, ndi angelo ake anaponyedwa naye pamodzi.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa