Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yeremiya 8:21 - Buku Lopatulika

21 Bala la mwana wamkazi wa anthu anga ndaphwetekwa nalo; ndada mtima; kudabwa kwandigwira.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

21 Bala la mwana wamkazi wa anthu anga ndaphwetekwa nalo; ndada mtima; kudabwa kwandigwira.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

21 Ndikumva kuŵaŵa chifukwa cha mavuto a anthu anga, ndikungolira, nkhaŵa yandigwira.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

21 Chifukwa cha mavuto a anthu anga, ine ndikumva kuwawa; ndikungolira ndipo mantha aakulu andigwira.

Onani mutuwo Koperani




Yeremiya 8:21
14 Mawu Ofanana  

Ndipo ndinati kwa mfumu, Mfumu ikhale ndi moyo kosatha; ilekerenji nkhope yanga kuchita chisoni, popeza pali bwinja kumzinda kuli manda a makolo anga, ndi zipata zake zopsereza ndi moto.


Ndipo udzati kwa iwo mau awa, Maso anga agwe misozi usana ndi usiku, asaleke; pakuti namwali mwana wa anthu anga wasweka ndi kusweka kwakukulu, ndi bala lopweteka kwambiri.


Yuda alira, ndipo zipata zake zilefuka, zikhala pansi zovekedwa ndi zakuda; mfuu wa Yerusalemu wakwera.


Koma ine, pokhala mbusa sindinafulumire kuchokerako kuti ndikutsateni Inu; sindinakhumbe tsiku la tsoka; Inu mudziwa, chimene chinatuluka pa milomo yanga chinali pamaso panu.


Matumbo anga, matumbo anga! Ndipoteka pamtima panga penipeni; mtima wanga sukhala pansi m'kati mwanga; sindithai kutonthola; pakuti wamva, moyo wanga, mau a lipenga, mbiri ya nkhondo.


Masika apita, mphakasa yatha, ndipo ife sitinapulumutsidwe.


Ha, mutu wanga ukadakhala madzi, ndi maso anga kasupe wa misozi, kuti usana ndi usiku ndilirire ophedwa a mwana wamkazi wa anthu anga!


Ine ndine munthuyu wakuona msauko ndi ndodo ya ukali wake.


Pamaso pao mitundu ya anthu ikumva zowawa, nkhope yonse zitumbuluka.


Ndiye mopanda kanthu mwakemo ndi mwachabe, ndi wopasuka; ndi mtima usungunuka, ndi maondo aombana, ndi m'zuuno zonse muwawa, ndi nkhope zao zatumbuluka.


Ndipo m'mene anayandikira, anaona mzindawo naulirira,


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa