Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yeremiya 6:8 - Buku Lopatulika

8 Ulangizidwe, Yerusalemu, ungakuchokere moyo wanga, ndingakuyese iwe bwinja, dziko losakhalamo anthu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

8 Ulangizidwe, Yerusalemu, ungakuchokere moyo wanga, ndingakuyese iwe bwinja, dziko losakhalamo anthu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

8 Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuwopa kuti chikondi changa pa iwe chingathe, ndipo ndingakusandutse dziko lachipululu, dziko lopanda anthu.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

8 Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”

Onani mutuwo Koperani




Yeremiya 6:8
23 Mawu Ofanana  

Tsono, mafumu inu, chitani mwanzeru; langikani, oweruza inu a dziko lapansi.


Popeza udana nacho chilangizo, nufulatira mau anga.


Wodala munthu amene mumlanga, Yehova; ndi kumphunzitsa m'chilamulo chanu;


Tamvera uphungu, nulandire mwambo, kuti ukhale wanzeru pa chimaliziro chako.


Gwira mwambo, osauleka; uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.


koma sanamvere, sanatchere khutu lao, koma anaumitsa khosi lao, kuti asamve asalandire langizo.


Ana a mikango anambangulira iye, nakweza mau; anapasula dziko lake, mizinda yake yatenthedwa, mulibenso wokhalamo.


Pakuti nditatembenuka, ndinalapa; nditalangizidwa, ndinamenya pa ntchafu yanga; ndinakhala ndi manyazi, inde, ndinapepulidwa, chifukwa ndinasenza chitonzo cha ubwana wanga.


Ndipo anandipatsa Ine mbuyo, si nkhope, ngakhale ndinawaphunzitsa, kuuka m'mamawa ndi kuwaphunzitsa, koma sanamvere kulangizidwa.


Iwe Yerusalemu, utsuke mtima wako kuchotsa zoipa kuti upulumuke. Maganizo ako achabe agona mwako masiku angati?


Chifukwa chake, ati Ambuye Mulungu, Taonani, mkwiyo wanga ndi ukali wanga udzathiridwa pamalo ano, pa anthu, ndi pa nyama, ndi pa mitengo ya m'munda, ndi pa zipatso zapansi; ndipo udzatentha osazima.


Ndipo udzati kwa iwo, Umene ndi mtundu wosamvera mau a Yehova Mulungu wao, wosalola kulangizidwa, choonadi chatha, chadulidwa pakamwa pao.


Ndipo ndidzaletsa m'mizinda ya Yuda, ndi m'miseu ya Yerusalemu, mau akukondwa ndi mau akusekera, ndi mau a mkwati ndi mau a mkwatibwi; pakuti dziko lidzasanduka bwinja.


Ndipo ndidzayesa Yerusalemu miyulu, mbuto ya ankhandwe; ndipo ndidzayesa mizinda ya Yuda bwinja, lopanda wokhalamo.


M'mwemo iye anawulula chigololo chake, navula umaliseche wake; pamenepo moyo wanga unaipidwa naye, monga umo moyo unaipidwira mkulu wake.


Pakuti mai wao anachita chigololo; iye amene anali ndi pakati pa iwo anachita chamanyazi; pakuti anati, Ndidzatsata ondikondawo, akundipatsa ine chakudya changa, ndi madzi anga, ubweya wanga, ndi thonje langa, mafuta anga, ndi chakumwa changa.


Angakhale alera ana ao, koma ndidzawasowetsa, wosatsala munthu; ndithunso tsoka iwowa, pamene ndiwachokera.


Pamenepo dzikoli lidzakondwera nao masabata ake, masiku onse a kupasuka kwake, pokhala inu m'dziko la adani anu; pamenepo dziko lidzapumula, ndi kukondwera nao masabata ake.


Ndinati, Zedi udzandiopa Ine, udzalola kulangizidwa, kuti pokhala pake pasaonongeke, monga mwa zonse ndamuikira; koma analawirira mamawa, navunditsa machitidwe ao onse.


Akadakhala nazo nzeru, akadazindikira ichi, akadasamalira chitsirizo chao!


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa