Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yeremiya 52:11 - Buku Lopatulika

11 Ndipo anakolowola maso a Zedekiya, ndipo mfumu ya ku Babiloni inammanga m'zigologolo, nimtengera ku Babiloni, nimuika m'ndende mpaka tsiku la kufa kwake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

11 Ndipo anakolowola maso a Zedekiya, ndipo mfumu ya ku Babiloni inammanga m'zigologolo, nimtengera ku Babiloni, nimuika m'ndende mpaka tsiku la kufa kwake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

11 Ndipo adamkolowola maso Zedekiyayo, nammanga ndi maunyolo nkupita naye ku Babiloni. Kumeneko adamuponya m'ndende kuti akhalemo moyo wake wonse.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

11 Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.

Onani mutuwo Koperani




Yeremiya 52:11
7 Mawu Ofanana  

Ndipo pambuyo pake, ati Yehova, ndidzapereka Zedekiya mfumu ya Yuda, ndi atumiki ake, ndi anthu, ngakhale a m'mzinda uwu amene asiyidwa ndi mliri, ndi lupanga, ndi njala, m'dzanja la Nebukadinezara mfumu ya ku Babiloni, ndi m'dzanja la adani ao, ndi m'dzanja la amene afuna moyo wao; ndipo adzawakantha ndi lupanga lakuthwa; osawaleka, osachita chisoni, osachita chifundo.


Ndipo anakolowola maso a Zedekiya, nammanga m'zigologolo, kunka naye ku Babiloni.


Wachotsa mwamphamvu dindiro lake ngati la m'munda; waononga mosonkhanira mwake; Yehova waiwalitsa anthu msonkhano ndi Sabata mu Ziyoni; wanyoza mfumu ndi wansembe mokwiya mwaukali.


Ndidzamphimba ndi ukonde wanga, nadzakodwa iye mu msampha wanga; ndipo ndidzafika naye ku Babiloni, ku dziko la Ababiloni; sadzaliona, chinkana adzafako.


Pali Ine, ati Ambuye Yehova, pamalo pokhala mfumu, imene idamchititsa ufumu, imene anapeputsa lumbiro lake, imene anathyola pangano lake, adzafa pamodzi ndi iye pakati pa Babiloni.


Ndipo adzakudzera ndi zida, magaleta a nkhondo, ndi magaleta ena, pamodzi ndi msonkhano wa mitundu ya anthu; adzadziikira pozungulira pako ndi zikopa zotchinjiriza ndi zisoti; ndipo ndidzawaika aweruze, nadzakuweruza monga mwa maweruzo ao.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa