Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yeremiya 51:62 - Buku Lopatulika

62 nuti, Inu Yehova, mwanena za malo ano, kuti mudzawatha, kuti asakhalemo, ngakhale anthu ngakhale nyama, koma akhale bwinja nthawi za nthawi.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

62 nuti, Inu Yehova, mwanena za malo ano, kuti mudzawatha, kuti asakhalemo, ngakhale anthu ngakhale nyama, koma akhale bwinja nthawi za nthawi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

62 Ukanene kuti, ‘Inu Chauta, mwalengeza cholinga chanu chofuna kuwononga malo ano, osasiyapo kanthu, munthu kapena nyama. Ndipo adzakhala chipululu mpaka muyaya.’

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

62 Ndipo ukanene kuti, ‘Inu Yehova, mwanena kuti mudzawononga malo ano, kotero kuti simudzatsala munthu kapena nyama mʼdziko muno; lidzakhala chipululu mpaka muyaya.’

Onani mutuwo Koperani




Yeremiya 51:62
16 Mawu Ofanana  

Ndipo kudzakhala, zitapita zaka makumi asanu ndi awiri, ndidzalanga mfumu ya ku Babiloni, ndi mtundu uja womwe, ati Yehova, chifukwa cha mphulupulu zao, ndi dziko la Ababiloni; ndipo ndidzaliyesa mabwinja amuyaya.


taonani, Ine, ndidzatuma ndi kutenga mabanja onse a kumpoto, ati Yehova, ndipo ndidzatuma kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babiloni, mtumiki wanga, ndipo ndidzatengera iwo padziko lino, ndi pa okhalamo ake onse, ndi pa mitundu iyi yozungulira, ndipo ndidzathetsa iwo ndithu, ndi kuwayesa iwo chizizwitso, ndi chotsonyetsa, ndi bwinja lamuyaya.


Yehova wa makamu atero: M'malo muno, muli bwinja, mopanda munthu ndi nyama, m'mizinda yake yonse, mudzakhalanso mokhalamo abusa ogonetsa zoweta zao.


amai anu adzakhala ndi manyazi ambiri; amene anakubalani adzathedwa nzeru; taonani, adzakhala wapambuyo wa amitundu, chipululu, dziko louma, bwinja.


Chifukwa cha mkwiyo wa Yehova sadzakhalamo anthu, koma padzakhala bwinja; onse akupita pa Babiloni adzadabwa, adzatsonyera pa zovuta zake zonse.


Pakuti mtundu wa anthu udzatuluka kumpoto kudzamenyana naye, udzachititsa dziko lake bwinja, losakhalamo anthu; athawa, apita, anthu ndi nyama.


Dziko linthunthumira ndi kuphwetekedwa, pakuti zimene Yehova analingalirira Babiloni zilipobe, zoti ayese dziko la Babiloni bwinja lopanda wokhalamo.


Ndipo Babiloni adzasanduka miunda, mokhala ankhandwe, chizizwitso, chotsonyetsa, wopanda okhalamo.


Mizinda yake yakhala bwinja, dziko louma, chipululu mosakhalamo anthu, mosapita mwana wa munthu aliyense.


Ndipo Yeremiya anati kwa Seraya, Pamene ufika ku Babiloni, samalira kuti uwerenge mau awa onse,


Ndidzakusandutsa mabwinja osatha; ndi m'mizinda mwako simudzakhalanso anthu; motero mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa