Yeremiya 49:3 - Buku Lopatulika3 Kuwa, iwe Hesiboni, pakuti Ai wapasuka; lirani, inu ana aakazi a Raba, muvale chiguduli; chitani maliro, thamangani kwina ndi kwina pamipanda; pakuti mfumu yao idzalowa m'ndende, ansembe ake ndi akulu ake pamodzi. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 20143 Kuwa, iwe Hesiboni, pakuti Ai wapasuka; lirani, inu ana akazi a Raba, muvale chiguduli; chitani maliro, thamangani kwina ndi kwina pamipanda; pakuti mfumu yao idzalowa m'ndende, ansembe ake ndi akulu ake pamodzi. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa3 “Lirani, inu a ku Hesiboni, pakuti mzinda wa Ai waonongeka. Lirani chokweza, inu ana aakazi a ku Raba. Valani ziguduli kuwonetsa chisoni, mulire, muthaŵire uku ndi uku m'kati mwa machinga. Ndithu, mulungu wanu Milikomu adzatengedwa ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndi akalonga ake. Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero3 “Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake. Onani mutuwo |