Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yeremiya 48:32 - Buku Lopatulika

32 Iwe mpesa wa Sibima; ndidzakulirira iwe ndi kulira kopambana kulira kwa Yazere, nthambi zako zinapitirira nyanja, zinafikira kunyanja ya Yazere; wakufunkha wagwera zipatso zako za mphakasa ndi mphesa zako.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

32 Iwe mpesa wa Sibima; ndidzakulirira iwe ndi kulira kopambana kulira kwa Yazere, nthambi zako zinapitirira nyanja, zinafikira kunyanja ya Yazere; wakufunkha wagwera zipatso zako za mpakasa ndi mphesa zako.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

32 Ndikulira anthu a ku Sibima kupambana m'mene ndidalirira anthu a ku Yazere. Iwe mzinda wa Sibima, uli ngati mpesa umene nthambi zake zidatambalala mpaka ku nyanja, kukafika mpaka ku Yazere. Woononga wasakaza zipatso zako zam'chilimwe, wasakaza mipesa yako yonse.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

32 Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri. Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja; zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri. Wowononga wasakaza zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.

Onani mutuwo Koperani




Yeremiya 48:32
13 Mawu Ofanana  

Koma ine, taonani, ndidzakhala pa Mizipa, ndiima pamaso pa Ababiloni, amene adzadza kwa ife; koma inu sonkhanitsani vinyo ndi zipatso zamalimwe ndi mafuta, muziike m'mbiya zanu, nimukhale m'mizinda imene mwailanda.


Mowabu wapasuka, akwera kulowa m'mizinda yake, ndi anyamata ake osankhika atsikira kukaphedwa, ati Mfumu, dzina lake ndiye Yehova wa makamu.


Iwe mwana wamkazi wokhala mu Diboni, utsike pa ulemerero wako, nukhale ndi ludzu; pakuti wakufunkha Mowabu wakukwerera, iwe waononga malinga ako.


Ndipo wakufunkha adzafikira pa mizinda yonse, sudzapulumuka mzinda uliwonse; chigwa chomwe chidzasakazidwa, ndipo chidikha chidzaonongedwa; monga wanena Yehova.


Ndipo Mose anatumiza anthu akazonde Yazere, nalanda midzi yake, napirikitsa Aamori a komweko.


Koma ana a Rubeni ndi ana Gadi anali nazo zoweta zambirimbiri; ndipo anapenyerera dziko la Yazere, ndi dziko la Giliyadi, ndipo taonani, malowo ndiwo malo a zoweta.


Ataroti, ndi Diboni, ndi Yazere, ndi Nimira, ndi Hesiboni, ndi Eleyale, ndi Sibima, ndi Nebo, ndi Beoni,


Ataroti-Sofani, Yazere, ndi Yogobeha;


ndi Nebo, ndi Baala-Meoni (anasintha maina ao), ndi Sibima; ndipo anaitcha mizinda adaimanga ndi maina ena.


ndi Kiriyataimu, ndi Sibima, ndi Zeretisahara, m'phiri la kuchigwa;


Ndipo malire ao ndiwo Yazere, ndi mizinda yonse ya Giliyadi, ndi dziko la ana a Amoni logawika pakati, mpaka ku Aroere, wokhala chakuno cha Raba;


Hesiboni ndi mabusa ake, Yazere ndi mabusa ake: yonse pamodzi mizinda inai.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa