Yeremiya 48:26 - Buku Lopatulika26 Umledzeretse iye; pakuti anadzikuza pokana Yehova; Mowabu yemwe adzamvimvinika m'kusanza kwake, ndipo iye adzasekedwanso. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 201426 Umledzeretse iye; pakuti anadzikuza pokana Yehova; Mowabu yemwe adzavimvinika m'kusanza kwake, ndipo iye adzasekedwanso. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa26 “Mledzeretseni Mowabu chifukwa adadzikuza poukira Chauta. Avimvinizike m'masanzi ake omwe. Akhale chinthu chomachiseka. Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero26 “Muledzeretseni Mowabu, chifukwa anadzikuza powukira Yehova. Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake; mulekeni akhale chinthu chomachiseka. Onani mutuwo |
koma munadzikweza kutsutsana naye Ambuye wa Kumwamba; ndipo anabwera nazo zotengera za nyumba yake kwa inu; ndi inu ndi akulu anu, akazi anu ndi akazi anu aang'ono, mwamweramo vinyo; mwalemekezanso milungu yasiliva, ndi yagolide, yamkuwa, yachitsulo, yamtengo, ndi yamwala, imene siiona kapena kumva, kapena kudziwa; ndi Mulungu amene m'dzanja mwake muli mpweya wanu, ndi njira zanu zonse, yemweyo simunamchitire ulemu.