Yeremiya 4:31 - Buku Lopatulika31 Pakuti ndamva kubuula ngati kwa mkazi wobala, ndi msauko ngati wa mkazi wobala mwana wake woyamba, mau a mwana wamkazi wa Ziyoni wakupuma mosiyiza, wakutambasula manja ake, ndi kuti, Tsoka ine tsopano! Pakuti moyo wanga walefuka chifukwa cha ambanda. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 201431 Pakuti ndamva kubuula ngati kwa mkazi wobala, ndi msauko ngati wa mkazi wobala mwana wake woyamba, mau a mwana wamkazi wa Ziyoni wakupuma mosiyiza, wakutambasula manja ake, ndi kuti, Tsoka ine tsopano! Pakuti moyo wanga walefuka chifukwa cha ambanda. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa31 Ndidamva kulira ngati kwa mkazi pa nthaŵi yake yochira, kubuula ngati kwa mkazi pa uchembere wake woyamba. Kumeneku kunali kulira kwa anthu a mu Ziyoni, ŵefuŵefu, atatambalitsa manja ao, akunena kuti, “Tsoka ife! Tikukomoka, moyo wathu waperekedwa kwa anthu otipha.” Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero31 Ndikumva kulira ngati kwa mayi pa nthawi yake yobereka, kubuwula ngati kwa mayi amene akubereka mwana wake woyamba. Kuliraku ndi kwa anthu a mu Ziyoni, wefuwefu. Atambalitsa manja awo nʼkumati, “Kalanga ife! Tikukomoka. Moyo wathu waperekedwa kwa anthu otipha.” Onani mutuwo |