Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yeremiya 4:25 - Buku Lopatulika

25 Ndinaona, ndipo taona, panalibe munthu, ndi mbalame zonse zakumwamba zinathawa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

25 Ndinaona, ndipo taona, panalibe munthu, ndi mbalame zonse zakumwamba zinathawa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

25 Ndidayang'ana, osaona ndi munthu mmodzi yemwe, ndipo mbalame zonse zamumlengalenga zinali zitathaŵa.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

25 Ndinayangʼana, ndipo sindinaone anthu; mbalame iliyonse ya mlengalenga inali itathawa.

Onani mutuwo Koperani




Yeremiya 4:25
6 Mawu Ofanana  

Dziko lidzalira masiku angati, nilifota therere la minda yonse? Chifukwa cha zoipa za iwo okhalamo, zithedwa zinyama, ndi mbalame; pakuti iwo anati, Iye sadzaona chitsiriziro chathu.


Chifukwa cha mapiri ndidzagwa misozi ndi kulira, chifukwa cha mabusa a chipululu ndidzachita maliro, chifukwa apserera, kuti anthu sangathe kupitirirapo; ndiponso anthu sangathe kumva mau a ng'ombe zao; mbalame za mlengalenga ndi nyama zathawa, zapita.


Kodi sindidzawalanga chifukwa cha izi? Ati Yehova; kodi moyo wanga sudzabwezera chilango mtundu wotere?


motero kuti nsomba za m'nyanja, ndi mbalame za m'mlengalenga, ndi nyama zakuthengo, ndi zokwawa zonse zakukwawa pansi, ndi anthu onse akukhala padziko, zidzanjenjemera pamaso panga; ndi mapiri adzagwetsedwa, ndi potsetsereka padzagumuka, ndi makoma onse adzagwa pansi.


Chifukwa chake dziko lidzachita chisoni, ndi aliyense wokhalamo adzalefuka, pamodzi ndi nyama zakuthengo, ndi mbalame za m'mlengalenga; ndi nsomba za m'nyanja zomwe zidzachotsedwa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa