Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yeremiya 38:21 - Buku Lopatulika

21 Koma ngati mukana kutuluka, mau anandisonyeza Yehova ndi awa:

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

21 Koma ngati mukana kutuluka, mau anandisonyeza Yehova ndi awa:

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

21 Koma mukakana kutuluka kuti mukadzipereke, Chauta wandiwululira kuti

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

21 Koma mukakana kudzipereka, chimene Yehova wandiwululira ndi ichi:

Onani mutuwo Koperani




Yeremiya 38:21
20 Mawu Ofanana  

nachita choipa pamaso pa Yehova Mulungu wake; sanadzichepetse kwa Yeremiya mneneri wakunena zochokera pakamwa pa Yehova.


Koma Iye ndiye wa mtima umodzi, adzambweza ndani? Ndi ichi chimene moyo wake uchifuna achichita.


Kodi chilango cha Mulungu chikhale monga muchifuna inu, pakuti muchikana? Musankhe ndi inu, ine ai; m'mwemo monga mudziwa, nenani.


Ndipo Yehova anati kwa Mose, Mukana kusunga zouza zanga ndi malamulo anga kufikira liti?


Koma mudziwe ndithu kuti, ngati mudzandipha ine, mudzadzitengera nokha mwazi wosachimwa, ndi pa mzinda uwu, ndi pa okhalamo ake; pakuti mwa ntheradi Yehova wandituma kwa inu kuti ndinene mau onse awa m'makutu anu.


Koma Yeremiya anati, Sadzakuperekani. Mveranitu mau a Yehova, amene ndinena ndi inu, chomwecho kudzakomera inu, ndipo moyo wanu udzakhalabe.


Taonani, akazi onse otsala m'nyumba ya mfumu ya Yuda adzatulutsidwa kunka kwa akulu a mfumu ya ku Babiloni, ndipo akaziwo adzati, Oyanjana nanu anakunyengani, ndi kukuposani inu, mapazi anu amire m'thope, abwerera m'mbuyo.


Yehova Inu, maso anu sali pachoonadi kodi? Munawapanda iwo, koma sanaphwetekedwe mtima; munawatha iwo, koma akana kudzudzulidwa; alimbitsa nkhope zao koposa mwala; akana kubwera.


Ndipo ukanene nao mau anga, ngakhale akamva kapena akaleka kumva; pakuti iwo ndiwo opanduka.


Chinkana Balaki akandipatsa nyumba yake yodzala ndi siliva ndi golide, sindikhoza kutumpha mau a Yehova, kuchita chokoma kapena choipa ine mwini wake; chonena Yehova ndicho ndidzanena ine?


Koma pamene iwo, anamkana, nachita mwano, anakutumula malaya ake, nati kwa iwo, Mwazi wanu ukhale pa mitu yanu; ine ndilibe kanthu; kuyambira tsopano ndinka kwa amitundu.


Penyani musakane wolankhulayo. Pakuti ngati iwowa sanapulumuke, pomkana Iye amene anawachenjeza padziko, koposatu sitidzapulumuka ife, odzipatulira kwa Iye wa Kumwamba;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa