Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yeremiya 37:2 - Buku Lopatulika

2 Koma ngakhale iye, ngakhale atumiki ake, ngakhale anthu a padziko, sanamvere mau a Yehova, amene ananena mwa Yeremiya mneneri.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

2 Koma ngakhale iye, ngakhale atumiki ake, ngakhale anthu a padziko, sanamvere mau a Yehova, amene ananena mwa Yeremiya mneneri.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

2 Koma Zedekiyayo ndi aphungu ake, pamodzi ndi anthu onse a m'dzikomo, sadamvere mau amene Chauta adalankhula kudzera mwa mneneri Yeremiya.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Koma Zedekiya kapena atumiki ake ngakhalenso anthu a mʼdzikomo sanasamalire mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa mneneri Yeremiya.

Onani mutuwo Koperani




Yeremiya 37:2
15 Mawu Ofanana  

Ndipo Davide anati, Ndidzachitira Hanuni mwana wa Nahasi zokoma, monga atate wake anandichitira ine zokoma. Chomwecho Davide anatumiza ndi dzanja la anyamata ake kuti akamsangalatse chifukwa cha atate wake. Ndipo anyamata a Davide anafika ku dziko la ana a Amoni.


natumiza ndi dzanja la Natani mneneriyo, namutcha dzina lake Wokondedwa ndi Yehova, chifukwa cha Yehova.


Ndipo anamuika, namlira Aisraele, monga mwa mau a Yehova anawalankhula padzanja la mtumiki wake Ahiya mneneri.


Ndiponso mau a Yehova anadza ndi dzanja la mneneri Yehu mwana wa Hanani, kutsutsa Baasa ndi nyumba yake, chifukwa cha zoipa zonse anazichita iye pamaso pa Yehova; popeza anaputa mkwiyo wake ndi machitidwe a manja ake, nafanana ndi nyumba ya Yerobowamu; ndiponso popeza anaikantha.


Zedekiya anali wa zaka makumi awiri mphambu chimodzi polowa ufumu wake, nakhala mfumu mu Yerusalemu zaka khumi ndi chimodzi,


Koma anati, Mverani, Ambuye, tumizani padzanja la iye amene mudzamtuma.


Wotumiza mau ndi dzanja la chitsiru adula mapazi ake, namwa zompweteka.


Mkulu akamvera chinyengo, atumiki ake onse ali oipa.


Yehova Mulungu wa Israele atero, Pita, nena kwa Zedekiya mfumu ya Yuda, numuuze iye, kuti Yehova atero, Taona, ndidzapereka mzindawu m'dzanja la mfumu ya ku Babiloni, ndipo adzautentha ndi moto;


Ndipo iwe wolasidwa woipa, kalonga wa Israele, amene lafika tsiku lako, nthawi ya mphulupulu yotsiriza;


Ndalankhulanso ndi aneneri, ndipo Ine ndachulukitsa masomphenya; ndi padzanja la aneneri ndinanena ndi mafanizo.


Ndipo Aroni ndi ana ake aamuna anachita zonse zimene Yehova analamula padzanja la Mose.


Chifukwa chake iye wotaya ichi, sataya munthu, komatu Mulungu, wakupatsa Mzimu wake Woyera kwa inu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa