Yeremiya 21:6 - Buku Lopatulika6 Ndipo ndidzakantha okhalamo m'mzinda uwu, anthu ndi nyama, adzafa ndi mliri waukulu. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 20146 Ndipo ndidzakantha okhalamo m'mudzi uwu, anthu ndi nyama, adzafa ndi chaola chachikulu. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa6 Ndidzakantha okhala mumzindamu ndi ziŵeto zomwe, ndipo zonse zidzafa ndi mliri woopsa. Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero6 Ndidzakantha amene amakhala mu mzinda muno, anthu pamodzi ndi zirombo, ndipo zidzafa ndi mliri woopsa. Onani mutuwo |
Pakuti Yehova atero, Taonani, ndidzakuyesa iwe choopsa cha kwa iwe mwini, ndi kwa abwenzi ako onse; ndipo iwo adzagwa ndi lupanga la adani ao, ndipo maso ako adzaona; ndipo ndidzapereka Ayuda onse m'dzanja la mfumu ya ku Babiloni, ndipo iye adzawatengera iwo am'nsinga ku Babiloni, nadzawapha ndi lupanga.