Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yeremiya 19:11 - Buku Lopatulika

11 nuziti kwa iwo, Yehova wa makamu atero: Chomwecho ndidzaphwanya anthu awa ndi mzinda uwu, monga aphwanya mbiya ya woumba, imene sangathe kuiumbanso, ndipo adzaika maliro mu Tofeti, mpaka mulibe malo akuikamo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

11 nuziti kwa iwo, Yehova wa makamu atero: Chomwecho ndidzaphwanya anthu awa ndi mudzi uwu, monga aphwanya mbiya ya woumba, imene sangathe kuiumbanso, ndipo adzaika maliro m'Tofeti, mpaka mulibe malo akuikamo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

11 Ndiye udzaŵauze kuti, Chauta Wamphamvuzonse akuti, Umu ndi m'mene ndidzaonongere anthu ameneŵa, monga momwe woumba amaphwanyira mbiya yake, kotero kuti sangathenso kuikonza. Anthu akufawo adzaŵaika ku Tofeti, chifukwa choti kwina kulikonse sikudzakhala malo oŵaika.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

11 ndipo ukawawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndidzaphwanya dziko lino ndi mzinda uno ngati momwe wowumba amaphwanyira mbiya yake ndipo sangathe kuyikonzanso. Adzayika anthu akufa ku Tofeti chifukwa padzasowa malo ena owayika.

Onani mutuwo Koperani




Yeremiya 19:11
13 Mawu Ofanana  

Udzawathyola ndi ndodo yachitsulo; udzawaphwanya monga mbiya ya woumba.


Chifukwa chake tsoka lake lidzadza modzidzimuka; adzasweka msangamsanga, palibe chompulumutsa.


Ndipo Iye adzagumulapo, monga mbiya ya woumba isweka, ndi kuiswaiswa osaileka; ndipo sipadzapezedwa m'zigamphu zake phale lopalira moto pachoso, ngakhale lotungira madzi padziwe.


Ndipo ndidzaphwanyanitsa wina ndi wina, atate ndi ana, ati Yehova; sindidzakhala ndi chisoni, sindidzapulumutsa, sindidzakhala ndi chifundo, chakuti ndisawaononge.


Ndidzatero ndi malo ano, ati Yehova, ndi okhalamo, kusanduliza mzinda uwu ngati Tofeti;


chifukwa chake, taonani, masiku adza, ati Yehova kuti pamalo pano sipadzatchedwanso Tofeti, kapena Chigwa cha mwana wake wa Hinomu, koma Chigwa Chophera anthu.


Kuwani, inu abusa, lirani, gubudukani, inu akulu a zoweta; pakuti masiku a kuphedwa kwanu akwanira ndithu, ndipo ndidzakuphwanyani inu, ndipo mudzagwa ngati chotengera chofunika.


Pamwamba pa matsindwi a Mowabu ndi m'miseu mwake muli kulira monsemonse; pakuti ndaswa Mowabu monga mbiya m'mene mulibe chikondwero, ati Yehova.


Ndipo padzakhala, utatha kuwerenga buku ili, ulimange ndi mwala, nuliponye pakati pa Yufurate;


Ana a Ziyoni a mtengo wapatali, olingana ndi golide woyengetsa, angoyesedwa ngati mbiya zadothi zozipanga manja a woumba.


Ndipo anadza kwa ife natenga lamba la Paulo, nadzimanga yekha manja ndi mapazi, nati, Atero Mzimu Woyera, Munthu mwini lamba ili, adzammanga kotero Ayuda a mu Yerusalemu, nadzampereka m'manja a amitundu.


ndipo adzawalamulira ndi ndodo yachitsulo, monga zotengera za woumba mbiya ziphwanyika mapale; monga Inenso ndalandira kwa Atate wanga;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa