Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yeremiya 17:17 - Buku Lopatulika

17 Musakhale wondiopsetsa ine; ndinu pothawira panga tsiku la choipa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

17 Musakhale wondiopsetsa ine; ndinu pothawira panga tsiku la choipa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

17 Musandichititse mantha. Inu nokha ndiye pothaŵira panga, tsoka likandigwera.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

17 Musandichititse mantha; ndinu pothawira panga pa tsiku la mavuto.

Onani mutuwo Koperani




Yeremiya 17:17
11 Mawu Ofanana  

Pakuti tsoka lochokera kwa Mulungu linandiopsa, ndi chifukwa cha ukulu wake sindinakhoza kanthu.


Wodala iye amene asamalira wosauka! Tsiku la tsoka Yehova adzampulumutsa.


Koma ine, ndidzaimbira mphamvu yanu; inde ndidzaimbitsa chifundo chanu mamawa, pakuti Inu mwakhala msanje wanga, ndi pothawirapo ine tsiku la nsautso yanga.


Inu Yehova, mphamvu yanga, ndi linga langa, pothawirapo panga tsiku la msauko, amitundu adzadza kwa Inu kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, ndipo adzati, Makolo athu analandira cholowa cha bodza lokha, zopanda pake ndi zinthu zosapindula nazo.


Inu Yehova, chiyembekezo cha Israele, onse amene akukusiyani Inu adzakhala ndi manyazi; onse ondichokera Ine adzalembedwa m'dothi, chifukwa asiya Yehova, kasupe wa madzi amoyo.


Wodala munthu amene akhulupirira Yehova, amene chikhulupiriro chake ndi Yehova.


Ndipo Yehova adzadzuma ali ku Ziyoni, ndi kumveketsa mau ake ali ku Yerusalemu; ndi thambo ndi dziko lapansi zidzagwedezeka; koma Yehova adzakhala chopulumukirako anthu adzakhala chopulumukirako anthu ake, ndi linga la ana a Israele.


Yehova ali wabwino, ndiye polimbikirapo tsiku la msauko; ndipo adziwa iwo omkhulupirira Iye.


Mwa ichi mudzitengere zida zonse za Mulungu, kuti mudzakhoza kuima chitsutsire pofika tsiku loipa, ndipo, mutachita zonse, mudzachilimika.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa