Yeremiya 11:19 - Buku Lopatulika19 Koma ine ndinanga mwanawankhosa wofatsa wotengedwa kukaphedwa; ndipo sindinadziwe kuti anandichitira ine chiwembu, kuti, Tiononge mtengo ndi zipatso zake, timdule iye padziko la amoyo, kuti dzina lake lisakumbukikenso. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 201419 Koma ine ndinanga mwanawankhosa wofatsa wotengedwa kukaphedwa; ndipo sindinadziwa kuti anandichitira ine chiwembu, kuti, Tiononge mtengo ndi zipatso zake, timdule iye pa dziko la amoyo, kuti dzina lake lisakumbukikenso. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa19 Ndidakhala ngati mwanawankhosa amene akupita naye kokamupha. Sindidadziŵe kuti chidaloza pa ine chiwembu chimene ankakonzekera nkumanena kuti, “Tiyeni tiwudule mtengowu ukali moyo. Tiyeni timuphe munthu ameneyu, kuti asadzakumbukikenso.” Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero19 Ndinali ngati mwana wankhosa wofatsa amene akupita naye kukamupha; sindinkadziwa kuti chiwembu chimene ankakonzekeracho chinkaloza ine. Iwo amati: “Tiyeni timuphe munthu ameneyu kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.” Onani mutuwo |
Ndipo atapita masabata makumi asanu ndi limodzi mphambu awiri wodzozedwayo adzalikhidwa, nadzakhala wopanda kanthu; ndi anthu a kalonga wakudzayo adzaononga mzinda ndi malo opatulika; ndi kutsiriza kwake kudzakhala kwa chigumula, ndi kufikira chimaliziro kudzakhala nkhondo; chipasuko chalembedweratu.