Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yakobo 1:24 - Buku Lopatulika

24 pakuti wadziyang'anira yekha, nachoka, naiwala pompaja nali wotani.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

24 pakuti wadziyang'anira yekha, nachoka, naiwala pompaja nali wotani.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

24 Tsono amati akadzipenya, amachokapo, posachedwa nkuiŵalako m'mene akuwonekera.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

24 Akadziyangʼana amachoka, nthawi yomweyo nʼkuyiwala mmene akuonekera.

Onani mutuwo Koperani




Yakobo 1:24
8 Mawu Ofanana  

Ndipo anazizwa anthuwo nanena, Ndiye munthu wotani uyu, pakuti ngakhale mphepo ndi nyanja zimvera Iye?


Ndipo onse amene anazimva anazisunga m'mtima mwao, nanena, Nanga mwana uyu adzakhala wotani? Pakuti dzanja la Ambuye linakhala pamodzi ndi iye.


Koma Mfarisi, amene adamuitana Iye, pakuona, ananena mwa yekha, nati, Akadakhala mneneri uyu akadazindikira ali yani, ndi wotani mkaziyo womkhudza Iye, chifukwa ali wochimwa.


kuti Uthenga Wabwino wathu sunadze kwa inu m'mau mokha, komatunso mumphamvu, ndi mwa Mzimu Woyera, ndi m'kuchuluka kwakukulu; monga mudziwa tinakhala onga otani mwa inu chifukwa cha inu.


Pakuti ngati munthu ali wakumva mau, wosati wakuchita, iyeyu afanana ndi munthu wakuyang'anira nkhope yake ya chibadwidwe chake m'kalirole;


Koma iye wakupenyerera m'lamulo langwiro, ndilo laufulu, natero chipenyerere, ameneyo, posakhala wakumva wakuiwala, komatu wakuchita ntchito, adzakhala wodala m'kuchita kwake.


Popeza izi zonse zidzakanganuka kotero, muyenera inu kukhala anthu otani nanga, m'mayendedwe opatulika ndi m'chipembedzo,


Pamenepo anati kwa Zeba ndi Zalimuna, Amunawo munawapha ku Tabori anali otani? Iwo nayankha, Monga iwe momwemo iwowa; yense wakunga mwana wa mfumu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa