Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Oweruza 16:3 - Buku Lopatulika

3 Koma Samisoni anagona mpaka pakati pa usiku, nauka pakati pa usiku, nagwira zitseko za pa chipata cha mzinda, ndi mphuthu ziwirizo, nazichotsa ndi mpiringidzo womwe, naziika pa mapewa ake, nakwera nazo pamwamba paphiri lili pandunji pa Hebroni.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 Koma Samisoni anagona mpaka pakati pa usiku, nauka pakati pa usiku, nagwira zitseko za pa chipata cha mudzi, ndi mphuthu ziwirizo, nazichotsa ndi mpiringidzo womwe, naziika pa mapewa ake, nakwera nazo pamwamba pa phiri lili pandunji pa Hebroni.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 Koma Samisoni adagona mpaka pakati pa usiku. Pakati pa usikupo adadzuka, nagwira zitseko zapachipata ndi mafuremu ake onse aŵiri. Adazizula pamodzi ndi mpiringidzo ndi zina zonse. Adazisenza pa phewa, napita nazo pamwamba pa phiri loyang'anana ndi Hebroni.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Koma Samsoni anangogonako mpaka pakati pa usiku. Kenaka pakati pa usiku anadzuka nagwira zitseko za chipata cha mzinda ndi maferemu ake awiri, ndipo anazizula zonse pamodzi ndi mpiringidzo womwe. Anazisenza pa mapewa pake napita nazo pamwamba pa phiri loyangʼanana ndi Hebroni.

Onani mutuwo Koperani




Oweruza 16:3
6 Mawu Ofanana  

Popeza adaswa zitseko zamkuwa, nathyola mipiringidzo yachitsulo.


Wothyola wakwera pamaso pao; iwo anathyola, napita kuchipata, natuluka pomwepo; ndi mfumu yao yapita pamaso pao, ndipo Yehova awatsogolera.


yemweyo Mulungu anamuukitsa, atamasula zowawa za imfa, mwakuti sikunali kotheka kuti Iye agwidwe nayo.


Koma wina anauza a ku Gaza, ndi kuti, Samisoni walowa kuno. Pamenepo anamzinga, namlalira usiku wonse pa chipata cha mzinda, nakhala chete usiku wonse ndi kuti, Tidikire mpaka kucha, pamenepo tidzamupha.


Ndipo pambuyo pake kunali kuti anakonda mkazi m'chigwa cha Soreki, dzina lake ndiye Delila.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa