Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Mlaliki 6:11 - Buku Lopatulika

11 Pokhala zinthu zambiri zingochulukitsa zachabe, kodi anthu aona phindu lanji?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

11 Pokhala zinthu zambiri zingochulukitsa zachabe, kodi anthu aona phindu lanji?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

11 Mau akachuluka, zopandapake zimachulukanso. Nanga munthu apindulapo chiyani?

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

11 Mawu akachuluka zopandapake zimachulukanso, nanga munthu zimamupindulira chiyani?

Onani mutuwo Koperani




Mlaliki 6:11
13 Mawu Ofanana  

Chifukwa chake kudzikuza kunga unyolo pakhosi pao; achivala chiwawa ngati malaya.


Pamenepo ndinati mumtima mwanga, Chomwe chigwera chitsiru nanenso chindigwera; nanga bwanji ndinapambana kukhala wanzeru? Pamenepo ndinati mumtima mwanga kuti ichinso ndi chabe.


Pakuti chomwe chigwera ana a anthu chigweranso nyamazo; ngakhale chowagwera nchimodzimodzi; monga winayo angofa momwemo zinazo zifanso; inde onsewo ali ndi mpweya umodzi; ndipo munthu sapambana nyama pakuti zonse ndi chabe.


Anthu onse sawerengeka, ngakhale onsewo anawalamulira; koma amene akudza m'mbuyo sadzakondwera naye. Ichinso ndi chabe ndi chosautsa mtima.


Pali mmodzi palibe wachiwiri; inde, alibe mwana ngakhale mbale; koma ntchito yake yonse ilibe chitsiriziro, ngakhale diso lake silikhuta chuma. Samati, Ndigwira ntchito ndi kumana moyo wanga zabwino chifukwa cha yani? Ichinso ndi chabe, inde, vuto lalikulu.


Pakuti monga mu unyinji wa maloto muli zachabe motero mochuluka mau; koma dziopa Mulungu.


Chomwe chinalipo chatchedwa dzina lake kale, chidziwika kuti ndiye munthu; sangathe kulimbana ndi womposa mphamvu.


Pakuti ndani adziwa chomwe chili chabwino kwa munthu ali ndi moyo masiku onse a moyo wake wachabe umene autsiriza ngati mthunzi? Pakuti ndani adzauza munthu chimene chidzaoneka m'tsogolo mwake kunja kuno?


Efuremu akudya mphepo, natsata mphepo ya kum'mawa; tsiku lonse achulukitsa mabodza ndi chipasuko, ndipo achita pangano ndi Asiriya, natenga mafuta kunka nao ku Ejipito.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa