Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Miyambo 4:4 - Buku Lopatulika

4 Atate nandiphunzitsa, nati kwa ine, mtima wako uumirire mau anga; sunga malamulo anga, nukhale ndi moyo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

4 Atate nandiphunzitsa, nati kwa ine, mtima wako uumirire mau anga; sunga malamulo anga, nukhale ndi moyo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

4 atatewo adandiphunzitsa ndi mau akuti, “Ugwiritse mumtima mwako zimene ndikukuuzazi, usunge malamulo anga, kuti ukhale ndi moyo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

4 Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.

Onani mutuwo Koperani




Miyambo 4:4
22 Mawu Ofanana  

Chifukwa ndamdziwa iye kuti alamulire ana ake ndi banja lake la pambuyo pake, kuti asunge njira ya Yehova, kuchita chilungamo ndi chiweruziro, kuti Yehova akamtengere Abrahamu chomwe anamnenera iye.


Ndipo iwe Solomoni mwana wanga, umdziwe Mulungu wa atate wako, umtumikire ndi mtima wangwiro ndi moyo waufulu; pakuti Yehova asanthula mitima yonse, nazindikira zolingirira zonse za maganizo; ukamfunafuna Iye udzampeza, koma ukamsiya Iye adzakusiya kosatha.


Ndinawabisa mau anu mumtima mwanga, kuti ndisalakwire Inu.


Mboni zanu ndizo zolungama kosatha; mundizindikiritse izi, ndipo ndidzakhala ndi moyo.


Ndinasamalira malangizo anu ndi mboni zanu; popeza njira zanga zonse zili pamaso panu.


Phunzitsa mwana poyamba njira yake; ndipo angakhale atakalamba sadzachokamo.


Mwananga, undipatse mtima wako, maso ako akondwere ndi njira zanga.


Mwananga, usaiwale malamulo anga, mtima wako usunge malangizo anga;


pakuti adzakuonjezera masiku ambiri, ndi zaka za moyo ndi mtendere.


Sunga malangizo anga, nukhale ndi moyo; ndi malamulo anga ngati mwana wa diso lako.


Tcherani khutu lanu, mudze kwa Ine, imvani, mzimu wanu nudzakhala ndi moyo; ndipo ndidzapangana nanu chipangano chosatha, ndicho zifundo zoona za Davide.


Koma Yeremiya anati, Sadzakuperekani. Mveranitu mau a Yehova, amene ndinena ndi inu, chomwecho kudzakomera inu, ndipo moyo wanu udzakhalabe.


Ndipo ndidziwa kuti lamulo lake lili moyo wosatha; chifukwa chake zimene ndilankhula, monga momwe Atate wanena ndi Ine, momwemo ndilankhula.


Ndipo atate inu, musakwiyitse ana anu; komatu muwalere iwo m'maleredwe ndi chilangizo cha Ambuye.


Chokhachi, dzichenjerani nokha, ndi kusunga moyo wanu mwachangu, kuti mungaiwale zinthuzi adaziona maso anu, ndi kuti zisachoke kumtima kwanu masiku onse a moyo wanu; koma muzidziwitsa ana anu ndi zidzukulu zanu.


Ndipo mau awa ndikuuzani lero, azikhala pamtima panu;


pokumbukira chikhulupiriro chosanyenga chili mwa iwe, chimene chinayamba kukhala mwa agogo ako Loisi, ndi mwa mai wako Yunisi, ndipo, ndakopeka mtima, mwa iwenso.


ndi kuti kuyambira ukhanda wako wadziwa malembo opatulika, okhoza kukupatsa nzeru kufikira chipulumutso, mwa chikhulupiriro cha mwa Khristu Yesu.


ndipo pamene anakonzeka wamphumphu anakhala kwa onse akumvera Iye chifukwa cha chipulumutso chosatha;


Nati Manowa, Achitike tsopano mau anu; koma makhalidwe ake a mwanayo ndi machitidwe ake adzatani?


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa