Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Mateyu 26:67 - Buku Lopatulika

67 Pomwepo iwo anathira malovu pankhope pake, nambwanyula Iye; ndipo ena anampanda khofu,

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

67 Pomwepo iwo anathira malovu pankhope pake, nambwanyula Iye; ndipo ena anampanda khofu,

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

67 Pomwepo iwo adayamba kumthira malovu kumaso nkumamumenya, ena kumamuwomba makofi,

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

67 Kenaka anamulavulira kumaso namumenya ndi zibakera. Ena anamumenya makofi.

Onani mutuwo Koperani




Mateyu 26:67
24 Mawu Ofanana  

Pamenepo Zedekiya mwana wa Kenana anasendera, napanda Mikaya patsaya, nati, Mzimu wa Yehova wandichokera bwanji, kulankhula ndi iwe?


Ndinapereka msana wanga kwa omenya, ndi masaya anga kwa iwo amene anakudzula tsitsi langa; sindinabisire nkhope yanga manyazi ndi kulavulidwa.


Monga ambiri anazizwa ndi iwe Israele, momwemo nkhope yake yaipitsidwa ndithu, kupambana munthu aliyense, ndi maonekedwe ake kupambana ana a anthu;


Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu; munthu wazisoni, ndi wodziwa zowawa; ndipo ananyozedwa monga munthu wombisira anthu nkhope zao; ndipo ife sitinamlemekeze.


Ndipo Pasuri anampanda Yeremiya mneneriyo, namuika matangadza amene anali mu Chipata cha Benjamini cha kumtunda, chimene chinali kunyumba ya Yehova.


Atembenuzire wompanda tsaya lake, adzazidwe ndi chitonzo.


Mwatiika pakati pa amitundu ngati zinyalala ndi za kudzala.


Uzisonkhana tsopano magulumagulu, mwana wamkazi wa magulu iwe; watimangira misasa, adzapanda woweruza wa Israele ndi ndodo patsaya.


Ndipo Yehova anati kwa Mose, Atate wake akadamlavulira malovu pankhope pake sakadachita manyazi masiku asanu ndi awiri? Ambindikiritse kunja kwa chigono masiku asanu ndi awiri; ndipo atatero amlandirenso.


nati, Utilote ife, Khristu Iwe; wakumenya Iwe ndani?


Namthira malovu, natenga bango, nampanda Iye pamutu.


koma ndinena kwa inu, Musakanize munthu woipa; koma amene adzakupanda iwe pa tsaya lako lamanja, umtembenuzire linanso.


ndipo adzamnyoza Iye, nadzamthira malovu, nadzamkwapula Iye, nadzamupha; ndipo pofika masiku atatu adzauka.


Ndipo ena anayamba kumthira malovu Iye, ndi kuphimba nkhope yake, ndi kumbwanyula, ndi kunena naye, Lota; ndipo anyamatawo anampanda Iye khofu.


Ndipo anampanda Iye pamutu pake ndi bango, namthira malovu, nampindira maondo, namlambira.


Koma m'mene Iye adanena izi, mmodzi wa anyamata akuimirirako anapanda Yesu khofu, ndi kuti, Kodi uyankha mkulu wa ansembe chomwecho?


nadza kwa Iye, nanena, Tikuoneni, mfumu ya Ayuda! Nampanda khofu.


ponamizidwa, tipempha; takhala monga zonyansa za dziko lapansi, litsiro la zinthu zonse, kufikira tsopano.


pamenepo mkazi wa mbale wake azimyandikiza pamaso pa akulu, nachotse nsapato yake ku phazi la mwamunayo, ndi kumthira malovu pankhope pake, ndi kumyankha ndi kuti, Atere naye mwamuna wosamanga nyumba ya mbale wake.


Yesu, ameneyo, chifukwa cha chimwemwe choikidwacho pamaso pake, anapirira mtanda, nanyoza manyazi, nakhala padzanja lamanja la mpando wachifumu wa Mulungu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa