Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 94:13 - Buku Lopatulika

13 kuti mumpumitse masiku oipa; kufikira atakumbira woipa mbuna.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

13 kuti mumpumitse masiku oipa; kufikira atakumbira woipa mbuna.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

13 Mumampumitsa pa nthaŵi yamavuto, mpaka woipa ataloŵa m'dzenje.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

13 mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 94:13
16 Mawu Ofanana  

Iye akapatsa mpumulo adzamtsutsa ndani? Akabisa nkhope yake adzampenyerera ndani? Chikachitika pa mtundu wa anthu, kapena pa munthu, nchimodzimodzi;


Ndidzaoperanji masiku oipa, pondizinga amphulupulu onditsata kuchidendene?


Koma Inu, Mulungu, mudzawatsitsira kudzenje la chionongeko. Anthu okhetsa mwazi ndi achinyengo masiku ao sadzafikira nusu; koma ine ndidzakhulupirira Inu.


Amitundu anagwa m'mbuna imene anaikumba, lakodwa phazi lao muukonde anautchera.


Kodi choipa chibwezedwe pa chabwino? Pakuti akumbira moyo wanga dzenje. Mukumbukire kuti ndinaima pamaso panu kuwanenera zabwino, kuwachotsera iwo ukali wanu.


Mfuu umvekedwe m'nyumba zao, pamene muwatengera khamu la nkhondo dzidzidzi; pakuti akumba dzenje lakundigwira ine, anabisira mapazi anga misampha.


Ndinamva, ndi m'mimba mwanga munabwadamuka, milomo yanga inanthunthumira pamau, m'mafupa mwanga mudalowa chivundi, ndipo ndinanjenjemera m'malo mwanga; kuti ndipumule tsiku lamsauko, pamene akwerera anthu kuti ayambane nao ndi makamu.


Momwemo utsalira mpumulo wa Sabata wa kwa anthu a Mulungu.


Ambuye adziwa kupulumutsa opembedza poyesedwa iwo, ndi kusunga osalungama kufikira tsiku loweruza akalangidwe;


Ndipo amitundu anakwiya, ndipo unadza mkwiyo wanu, ndi nthawi ya akufa yakuti aweruzidwe, ndi yakupereka mphotho akapolo anu aneneriwo, ndi oyera mtima, ndi iwo akuopa dzina lanu, ang'ono ndi akulu; ndi kuononga iwo akuononga dziko.


Ndipo ndinamva mau ochokera Kumwamba, ndi kunena, Lemba, Odala akufa akumwalira mwa Ambuye, kuyambira tsopano; inde, anena Mzimu, kuti akapumule ku zolemetsa zao; pakuti ntchito zao zitsatana nao pamodzi.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa