Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 78:70 - Buku Lopatulika

70 Ndipo anasankha Davide mtumiki wake, namtenga kumakola a nkhosa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

70 Ndipo anasankha Davide mtumiki wake, namtenga kumakola a nkhosa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

70 Mulungu adasankhula Davide mtumiki wake, ndipo adakamtenga ku makola a nkhosa.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

70 Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 78:70
13 Mawu Ofanana  

chitani tsono, popeza Yehova analankhula za Davide, kuti, Ndi dzanja la Davide mnyamata wanga ndidzapulumutsa anthu anga Aisraele ku dzanja la Afilisti, ndi ku dzanja la adani ao onse.


Koma Davide ananena ndi Mikala, Ndatero pamaso pa Yehova, amene anandisankha ine ndi kupitirira atate wako ndi banja lake lonse, nandiika ndikhale mtsogoleri wa anthu a Yehova, wa Israele, chifukwa chake ndidzasewera pamaso pa Yehova.


Chifukwa chake tsono udzatero kwa mtumiki wanga Davide, Atero Yehova wa makamu, Ndinakuchotsa kubusako kumene unalikutsata nkhosa kuti udzakhale mfumu ya anthu anga, ndiwo Israele.


Kuyambira tsiku lakutulutsa Ine anthu anga Aisraele m'dziko la Ejipito, sindinasankhe mzinda uliwonse mwa mafuko onse a Israele kumangamo nyumba yokhalamo dzina langa, koma ndinasankha Davide kukhala mfumu ya anthu anga Aisraele.


Koma Mose analikuweta gulu la Yetero mpongozi wake, wansembe wa ku Midiyani; natsogolera gululo m'tsogolo mwa chipululu, nafika kuphiri la Mulungu, ku Horebu.


Tiye tsopano, ndikutuma kwa Farao, kuti utulutse anthu anga, ana a Israele mu Ejipito.


Ndipo m'mene atamchotsa iye, anawautsira Davide akhale mfumu yao; amenenso anamchitira umboni, nati, Ndapeza Davide, mwana wa Yese, munthu wa pamtima panga, amene adzachita chifuniro changa chonse.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa