Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 73:19 - Buku Lopatulika

19 Ha? M'kamphindi ayesedwa bwinja; athedwa konse ndi zoopsa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

19 Ha? M'kamphindi ayesedwa bwinja; athedwa konse ndi zoopsa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

19 Adzangoferatu ndi mantha, ndi kuwonongeka pa kamphindi kochepa.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 73:19
18 Mawu Ofanana  

M'makutu mwake mumveka zoopsetsa; pali mtendere amfikira wakumuononga.


Zoopetsa zidzamchititsa mantha monsemo, nadzampirikitsa kumbuyo kwake.


kuti kufuula kokondwera kwa woipa sikukhalira kutha, ndi chimwemwe cha wonyoza Mulungu chikhala kamphindi?


Miphika yanu isanagwire moto waminga, adzaiuluza, yaiwisi ndi yoyaka.


Woipa athawa palibe momthamangitsa; koma olungama alimba mtima ngati mkango.


Pakuti munthu sadziwatu mphindi yake; monga nsomba zigwidwa mu ukonde woipa, ndi mbalame zikodwa mumsampha, momwemo ana a anthu amagwidwa ndi nthawi ya tsoka, ngati msampha umene uwagwera modzidzimuka.


chifukwa chake kuipa kumeneku kudzakhala kwa inu monga pogumuka pofuna kugwa, monga potukuka m'khoma lalitali, kugumuka kwake kufika modzidzimutsa dzidzidzi.


Chifukwa chake choipa chidzafika pa iwe; sudzadziwa kucha kwake, ndipo chionongeko chidzakugwera; sudzatha kuchikankhira kumbali; ndipo chipasuko chosachidziwa iwe chidzakugwera mwadzidzidzi.


Pamenepo padasandulika pa nkhope pake pa mfumu, ndi maganizo ake anamsautsa, ndi mfundo za m'chuuno mwake zinaguluka, ndi maondo ake anaombana.


Dzipatuleni pakati pa khamu lino, kuti ndiwathe m'kamphindi.


ameneyo, woperekedwa ndi uphungu woikidwa ndi kudziwiratu kwa Mulungu, inu mwampachika ndi kumupha ndi manja a anthu osaweruzika;


Pamene angonena, Mtendere ndi mosatekeseka, pamenepo chionongeko chobukapo chidzawagwera, monga zowawa mkazi wa pakati; ndipo sadzapulumuka konse.


chifukwa chakuopa chizunzo chake, nanena, Tsoka, tsoka, mzinda waukuluwo, Babiloni, mzinda wolimba! Pakuti mu ora limodzi chafika chiweruziro chanu.


Ndipo kunali, atapita masiku khumi, Yehova anamkantha Nabala, nafa.


Pomwepo Saulo anagwa pansi tantha, naopa kwakukulu, chifukwa cha mau a Samuele; ndipo analibe mphamvu; pakuti tsiku lonse ndi usiku wake wonse anakhala osadya kanthu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa