Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 49:13 - Buku Lopatulika

13 Njira yao ino ndiyo kupusa kwao, koma akudza m'mbuyo avomereza mau ao.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

13 Njira yao yino ndiyo kupusa kwao, koma akudza m'mbuyo avomereza mau ao.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

13 Zimenezi ndizo zimene zimaŵagwera anthu amene ali ndi chikhulupiriro chopusa, ndiwo mathero ake a onse amene amatsata maganizo otere.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

13 Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. Sela

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 49:13
6 Mawu Ofanana  

Pakuti chomwe chigwera ana a anthu chigweranso nyamazo; ngakhale chowagwera nchimodzimodzi; monga winayo angofa momwemo zinazo zifanso; inde onsewo ali ndi mpweya umodzi; ndipo munthu sapambana nyama pakuti zonse ndi chabe.


Koma tidzachita ndithu mau onse anatuluka m'kamwa mwathu, kufukizira mfumu yaikazi ya kumwamba, ndi kumthirira iye nsembe zothira, monga momwe tinkachitira ife, ndi atate athu, ndi mafumu athu ndi akulu athu, m'mizinda ya Yuda, ndi m'miseu ya Yerusalemu, pakuti pamenepo tinali ndi chakudya chokwanira, tinakhala bwino, sitinaona choipa.


Koma Mulungu anati kwa iye, Wopusa iwe, usiku womwe uno udzafunidwa moyo wako; ndipo zinthu zimene unazikonza zidzakhala za yani?


Pakuti nzeru ya dziko lino lapansi ili yopusa kwa Mulungu. Pakuti kwalembedwa, Iye agwira anzeru m'chenjerero lao;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa