Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 46:11 - Buku Lopatulika

11 Yehova wa makamu ali ndi ife, Mulungu wa Yakobo ndiye pamsanje pathu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

11 Yehova wa makamu ali ndi ife, Mulungu wa Yakobo ndiye pamsanje pathu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

11 Chauta Wamphamvuzonse ali nafe, Mulungu wa Yakobe ndiye kothaŵira kwathu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

11 Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife, Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 46:11
10 Mawu Ofanana  

Ndipo munthu uja wa Mulungu anafikako, nalankhula ndi mfumu ya Israele, nati, Atero Yehova, Popeza Aaramu amati, Yehova ndiye Mulungu wa kumapiri, osati Mulungu wa kuzigwa, mwa ichi ndidzapereka unyinji uwu waukulu m'dzanja mwako, kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova.


nati, Yehova Mulungu wa makolo athu, Inu sindinu Mulungu wa mu Mwamba kodi? Sindinu woweruza maufumu onse a amitundu kodi? Ndi m'dzanja mwanu muli mphamvu yolimba; palibe wina wakulimbana ndi Inu.


Anampempha, ndipo anapembedzeka, namvera kupembedza kwake, nambwezera ku Yerusalemu mu ufumu wake. Pamenepo anadziwa Manase kuti Yehova ndiye Mulungu.


Mulungu ndiye pothawirapo pathu ndi mphamvu yathu, thandizo lopezekeratu m'masautso.


Yehova wa makamu ali ndi ife; Mulungu wa Yakobo ndiye pamsanje pathu.


Mulungu adziwika m'zinyumba zake ngati msanje.


Maso a munthu akuyang'anira kumwamba adzatsitsidwa, ndi kudzikweza kwa anthu kudzaweramitsidwa pansi; ndipo Yehova yekha adzakwezedwa tsiku limenelo.


Ndipo kudzikweza kwa munthu kudzaweramitsidwa pansi, kudzikuza kwa munthu kudzatsitsidwa; ndipo Yehova yekha adzakwezedwa tsiku limenelo.


Inu Yehova, mphamvu yanga, ndi linga langa, pothawirapo panga tsiku la msauko, amitundu adzadza kwa Inu kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, ndipo adzati, Makolo athu analandira cholowa cha bodza lokha, zopanda pake ndi zinthu zosapindula nazo.


Mulungu wamuyaya ndiye mokhaliramo mwako; ndi pansipo pali manja osatha. Ndipo aingitsa mdani pamaso pako, nati, Ononga.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa