Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 44:14 - Buku Lopatulika

14 Mutiika tikhale onyozeka mwa amitundu, ndi kuti anthu atipukusire mitu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

14 Mutiika tikhale onyozeka mwa amitundu, ndi kuti anthu atipukusire mitu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

14 Inu mwatisandutsa anthu oŵanyodola pakati pa anthu a mitundu ina, anthu omangosekedwa pakati pa anzathu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

14 Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 44:14
15 Mawu Ofanana  

pamenepo Ine ndidzalikha Aisraele kuwachotsera m'dziko ndidawapatsali; ndipo nyumba ino ndapatulira dzina langayi ndidzaitaya kosapenyeka; ndipo Israele adzakhala ngati mwambi ndi nkhani pakati pa anthu onse.


Mau a Yehova akumnenera iye ndi awa, Namwali mwana wamkazi wa Ziyoni akunyoza, akuseka mwana wamkazi wa Yerusalemu, akupukusira mutu pambuyo pako.


pamenepo ndidzawazula m'dziko langa limene ndinawapatsa; ndi nyumba ino ndinaipatulira dzina langa ndidzaitaya, osaionanso, ndi kuiyesa mwambi ndi mnyozo mwa mitundu yonse ya anthu.


Pamenepo ndinanena nao, Muona choipa m'mene tilimo, kuti Yerusalemu ali bwinja, ndi zipata zake zotentha ndi moto; tiyeni timange linga la Yerusalemu, tisakhalenso chotonzedwa.


Inenso ndikadanena monga inu, moyo wanu ukadakhala m'malo mwa moyo wanga, ndikadalumikizanitsa mau akutsutsana nanu, ndi kukupukusirani mutu wanga.


Anandiyesanso chitonzo cha anthu; ndipo ndakhala ngati munthu womthira malovu pankhope pake.


Ndiwakhaliranso chotonza; pakundiona apukusa mutu.


Mutichitire chifundo, Yehova, mutichitire chifundo; pakuti takhuta kwambiri ndi mnyozo.


Onse akundipenya andiseka; akwenzula, apukusa mutu, nati,


Takhala chotonza cha anansi athu, ndi choseketsa ndi cholalatitsa iwo akutizinga.


awa ndiwo mau amene Yehova wanena za iye, Namwali, mwana wamkazi wa Ziyoni, wakunyoza iwe ndi kuseka iwe ndi chiphwete; mwana wamkazi wa Yerusalemu wapukusa mutu wake pambuyo pako.


Ndipo ndidzawapatsa akhale choopsetsa choipa ku maufumu a dziko lapansi; akhale chitonzo ndi nkhani ndi choseketsa, ndi chitemberero, monse m'mene ndidzawapirikitsiramo.


Pakuti asunga malemba a Omuri, ndi ntchito za nyumba ya Ahabu, ndipo mumayenda mu uphungu wao; kuti ndikusandulize bwinja, ndi okhalamo chotsonya; ndipo mudzasenza chitonzo cha anthu anga.


Ndipo mudzakhala chodabwitsa, ndi nkhani, ndi mwambi, mwa mitundu yonse ya anthu amene Yehova akutsogoleraniko.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa