Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 126:4 - Buku Lopatulika

4 Bwezani ukapolo wathu, Yehova, ngati mitsinje ya kumwera.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

4 Bwezani ukapolo wathu, Yehova, ngati mitsinje ya kumwera.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

4 Tibwezereni ufulu wathu, Inu Chauta, tikhale ngati mitsinje yam'chipululu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

4 Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 126:4
9 Mawu Ofanana  

Pobweza Yehova ukapolo wa Ziyoni, tinakhala ngati anthu akulota.


Mutibweze, Mulungu wa chipulumutso chathu, nimuletse udani wanu wa pa ife.


Pamenepo wopunduka adzatumpha ngati nswala, ndi lilime la wosalankhula lidzaimba; pakuti m'chipululu madzi adzatuluka, ndi mitsinje m'dziko loti see.


Ndidzagwetsa mitsinje pazitunda zoti see, ndi akasupe pakati pa zigwa; ndidzasandutsa chipululu, chikhale thamanda lamadzi, ndi mtunda wouma ukhale magwero a madzi.


Taonani, Ine ndidzachita chinthu chatsopano; tsopano chidzaoneka; kodi simudzachidziwa? Ndidzakonzadi njira m'chipululu, ndi mitsinje m'zidalala.


Ndipo ndidzapezedwa ndi inu, ati Yehova, ndidzabwezanso undende wanu, ndipo ndidzasonkhanitsa inu kwa mitundu yonse, ndi kumalo konse kumene ndinakupirikitsirani inu, ati Yehova; ndipo ndidzakubwezeraninso kumalo kumene ndinakutengani inu andende.


Pakuti, taona, masiku adzadza, ati Yehova, amene ndidzabwezanso undende wa anthu anga Aisraele ndi Ayuda, ati Yehova; ndipo ndidzawabwezera kudziko limene ndinapatsa makolo ao. Ndipo adzakhala nalo.


Ndipo ana a Yuda ndi ana a Israele adzasonkhanidwa pamodzi, nadzadziikira mkulu mmodzi, nadzakwera kuchoka m'dziko; pakuti tsiku la Yezireele ndi lalikulu.


pamenepo madzi ochokera kumagwero anaima, nauka ngati mulu, kutalitu ku Adama, ndiwo mzinda wa ku mbali ya Zaretani; koma madzi akutsikira kunka ku nyanja ya chidikha, ndiyo Nyanja ya Mchere, anadulidwa konse; ndipo anthu anaoloka pandunji pa Yeriko.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa