Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 119:96 - Buku Lopatulika

96 Ndinapenya malekezero ake a ungwiro wonse; koma lamulo lanu ndi lotakasuka ndithu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

96 Ndinapenya malekezero ake a ungwiro wonse; koma lamulo lanu ndi lotakasuka ndithu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

96 Ndazindikira kuti zabwino zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe konse malire.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 119:96
23 Mawu Ofanana  

Ndipo mu Israele monse munalibe wina anthu anamtama kwambiri chifukwa cha kukongola kwake monga Abisalomu; kuyambira ku mapazi kufikira pakati pamutu wake mwa iye munalibe chilema.


Ndipo uphungu wa Ahitofele anaupangira masiku aja, unali monga ngati munthu anafunsira mau kwa Mulungu; uphungu wonse wa Ahitofele unali wotere kwa Davide ndi kwa Abisalomu yemwe.


Ndipo Ahitofele, pakuona kuti sautsata uphungu wake anamanga bulu wake, nanyamuka, nanka kumzinda kwao, nakonza za pa banja lake, nadzipachika, nafa, naikidwa m'manda a atate wake.


Pomwepo Yowabu anati, Sindiyenera kuchedwa nawe. Natenga mikondo itatu nagwaza nayo mtima wa Abisalomu alikukhala wamoyo pakati pa mtengowo.


Ndipo anatenga Abisalomu namponya m'chidzenje chachikulu kunkhalangoko; naunjika pamwamba pake mulu waukulu ndithu wamiyala; ndipo Aisraele onse anathawa yense ku hema wake.


Chabe zachabetu, ati Mlalikiyo; zonse ndi chabe.


Pamenepo ndinayang'ana zonse manja anga anazipanga, ndi ntchito zonse ndinasauka pozigwira; ndipo taona, zonse zinali zachabechabe ndi kungosautsa mtima, ndipo kunalibe phindu kunja kuno.


Pakuti kulibe wolungama pansi pano amene achita zabwino osachimwa.


Thambo ndi dziko lapansi zidzachoka, koma mau anga sadzachoka ai.


Pakuti indetu ndinena kwa inu, Kufikira litapitirira thambo ndi dziko, kalemba kakang'ono kamodzi kapena kansonga kake kamodzi sikadzachokera kuchilamulo, kufikira zitachitidwa zonse.


koma Ine ndinena kwa inu, kuti yense wakuyang'ana mkazi kumkhumba, pamenepo watha kuchita naye chigololo mumtima mwake.


Pakuti tidziwa kuti chilamulo chili chauzimu; koma ine ndili wathupi, wogulitsidwa kapolo wa uchimo.


Naima iye naitana makamu a nkhondo a Israele, nanena nao, Munatulukiranji kundandalitsa nkhondo yanu? Sindine Mfilisti kodi, ndi inu anyamata a Saulo? Mudzisankhire munthu, atsikire kwa ine.


Iye anali ndi mwana wamwamuna dzina lake Saulo, mnyamata wokongola; pakati pa anthu onse a Israele panalibe wina wokongola ngati iye; anali wamtali, anthu ena onse anamlekeza m'chifuwa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa