Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 119:10 - Buku Lopatulika

10 Ndinakufunani ndi mtima wanga wonse; ndisasokere kusiyana nao malamulo anu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

10 Ndinakufunani ndi mtima wanga wonse; ndisasokere kusiyana nao malamulo anu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse, musalole kuti ndisiye kumvera malamulo anu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 119:10
25 Mawu Ofanana  

Ndipo Yuda yense anakondwera nalo lumbirolo; pakuti adalumbira ndi mtima wao wonse, namfunafuna ndi khumbo lao lonse; ndipo anampeza; ndi Yehova anawapumulitsa pozungulirapo.


Mupepula onse akusokera m'malemba anu; popeza chinyengo chao ndi bodza.


Khazikitsani mapazi anga m'mau anu; ndipo zisandigonjetse zopanda pake zilizonse.


Ndinasochera ngati nkhosa yotayika; funani mtumiki wanu; pakuti sindiiwala malamulo anu.


Odala iwo akusunga mboni zake, akumfuna ndi mtima wonse;


Munadzudzula odzikuza otembereredwa, iwo akusokera kusiyana nao malamulo anu.


Mundizindikiritse, ndipo ndidzasunga malamulo anu; ndidzawasamalira ndi mtima wanga wonse.


Ndinapemba pankhope panu ndi mtima wanga wonse: Mundichitire chifundo monga mwa mau anu.


Odzikuza anandipangira bodza: Ndidzasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.


Koma iwo akupatula kutsata njira zao zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi ochita zopanda pake. Mtendere ukhale pa Israele.


Atsitsimutsa moyo wanga; anditsogolera m'mabande a chilungamo, chifukwa cha dzina lake.


Popeza mtima wao sunakonzekere Iye, ndipo sanakhazikike m'chipangano chake.


akusiya mayendedwe olungama, akayende m'njira za mdima;


Munthu wosochera panjira ya nzeru adzakhala m'msonkhano wa akufa.


Ndipo kudzakhala khwalala kumeneko, ndi njira, ndipo idzatchedwa njira yopatulika; odetsedwa sadzapita m'menemo; koma Iye adzakhala nao oyenda m'njira, ngakhale opusa, sadzasochera m'menemo.


Ndipo zingakhale zonsezi Yuda mphwake wonyenga sanabwere kwa Ine ndi mtima wake wonse, koma monama, ati Yehova.


Nkhosa zanga zinasokera kumapiri ali onse, ndi pa chitunda chilichonse chachitali; inde nkhosa zanga zinabalalika padziko lonse lapansi, ndipo panalibe wakuzipwaira kapena kuzifunafuna.


Mtima wao wagawikana, tsopano adzapezeka opalamula, adzapasula maguwa ao a nsembe, nadzaononga zoimiritsa zao.


Palibe munthu angathe kukhala kapolo wa ambuye awiri: pakuti pena adzamuda mmodziyo, ndi kukonda winayo; pena adzakangamira kwa mmodzi, nadzanyoza wina. Simungathe kukhala kapolo wa Mulungu ndi wa Chuma.


Akapolo inu, mverani m'zonse iwo amene ali ambuye monga mwa thupi, wosati ukapolo wa pamaso, monga okondweretsa anthu, komatu ndi mtima wakulinga kumodzi, akuopa Ambuye;


Musakonde dziko lapansi, kapena za m'dziko lapansi. Ngati wina akonda dziko lapansi, chikondi cha Atate sichili mwa iye.


Ndipo Samuele analankhula ndi banja lonse la Israele nati, Ngati mukuti mubwerere kunka kwa Yehova ndi mitima yanu yonse, chotsani pakati pa inu milungu yachilendo, ndi Asitaroti, nimukonzere Yehova mitima yanu, ndi kumtumikira Iye yekha; mukatero, Iye adzakupulumutsani m'manja a Afilisti.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa