Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Marko 15:19 - Buku Lopatulika

19 Ndipo anampanda Iye pamutu pake ndi bango, namthira malovu, nampindira maondo, namlambira.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

19 Ndipo anampanda Iye pamutu pake ndi bango, namthira malovu, nampindira maondo, namlambira.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

19 Ankamumenya m'mutu ndi ndodo, namamthira malovu, nkumamugwadira monyodola.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

19 Ndipo anamugogoda pa mutu mobwerezabwereza ndi ndodo ndi kumulavulira. Anamugwadira ndi kumulambira Iye.

Onani mutuwo Koperani




Marko 15:19
32 Mawu Ofanana  

Ndipo panali pamene anamva mauwo mnyamata wa Abrahamu, anamgwadira Yehova pansi.


Ndipo iwo anati, Kapolo wanu atate wathu ali bwino, alipo. Ndipo anawerama, namgwadira iye.


Ndiponso ndidasiya mu Israele anthu zikwi zisanu ndi ziwiri osagwadira Baala maondo ao, osampsompsona ndi milomo yao.


Nchokoma kodi kuti Iye akusanthuleni? Kodi mudzamnyenga Iye monga munyenga munthu?


Okhala pachipata akamba za ine; ndipo oledzera andiimba.


Ndadzilumbira ndekha, mau achokera m'kamwa mwanga m'chilungamo, ndipo sadzabwerera, kuti mabondo onse adzandigwadira Ine, malilime onse nadzalumbira Ine.


Atero Yehova, Mombolo wa Israele, ndi Woyera wake, kwa Iye amene anthu amnyoza, kwa Iye amene mtundu wathu unyasidwa naye, kwa mtumiki wa olamulira: Mafumu adzaona, nadzauka; akalonga nadzalambira chifukwa cha Yehova, amene ali wokhulupirika, ngakhale Woyera wa Israele, amene anakusankha Iwe.


Ndinapereka msana wanga kwa omenya, ndi masaya anga kwa iwo amene anakudzula tsitsi langa; sindinabisire nkhope yanga manyazi ndi kulavulidwa.


Monga ambiri anazizwa ndi iwe Israele, momwemo nkhope yake yaipitsidwa ndithu, kupambana munthu aliyense, ndi maonekedwe ake kupambana ana a anthu;


Uzisonkhana tsopano magulumagulu, mwana wamkazi wa magulu iwe; watimangira misasa, adzapanda woweruza wa Israele ndi ndodo patsaya.


Namthira malovu, natenga bango, nampanda Iye pamutu.


ndipo adzamnyoza Iye, nadzamthira malovu, nadzamkwapula Iye, nadzamupha; ndipo pofika masiku atatu adzauka.


Ndipo ena anayamba kumthira malovu Iye, ndi kuphimba nkhope yake, ndi kumbwanyula, ndi kunena naye, Lota; ndipo anyamatawo anampanda Iye khofu.


Ndipo anayamba kumlankhula Iye, kuti, Tikuoneni, mfumu ya Ayuda!


Ndipo atatha kumnyoza anamvula chibakuwacho namveka Iye zovala zake. Ndipo anatuluka naye kuti akampachike Iye pamtanda.


Ndipo Iye ananena nao, Eliya ayamba kudza ndithu, nadzakonza zinthu zonse; ndipo kwalembedwa bwanji za Mwana wa Munthu, kuti ayenera kumva zowawa zambiri ndi kuyesedwa chabe?


Ndipo amuna amene analikusunga Yesu anamnyoza Iye, nampanda.


Ndipo Herode ndi asilikali ake anampeputsa Iye, namnyoza, namveka Iye chofunda chonyezimira, nambwezera kwa Pilato.


Ndipo asilikalinso anamnyoza, nadza kwa Iye, nampatsa vinyo wosasa,


Koma kuyankha kwa Mulungu kudatani kwa iye? Ndinadzisiyira ndekha anthu aamuna zikwi zisanu ndi ziwiri, amene sanagwadire Baala.


kuti m'dzina la Yesu bondo lililonse lipinde, la za m'mwamba ndi za padziko, ndi za pansi padziko,


Chifukwa chake titulukire kwa Iye kunja kwa tsasa osenza tonzo lake.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa