Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Marko 13:31 - Buku Lopatulika

31 Thambo ndi dziko lapansi zidzapita; koma mau anga sadzapita.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

31 Thambo ndi dziko lapansi zidzapita; koma mau anga sadzapita.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

31 Thambo ndi dziko lapansi zidzatha, koma mau anga sadzatha mphamvu konse.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

31 Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”

Onani mutuwo Koperani




Marko 13:31
18 Mawu Ofanana  

Awa ndi mau a Yehova anawanena ndi Yehu, ndi kuti, Ana ako kufikira mbadwo wachinai adzakhala pa mpando wachifumu wa Israele. Ndipo kunatero momwemo.


Malamulo a Yehova ali angwiro, akubwezera moyo; mboni za Yehova zili zokhazikika, zakuwapatsa opusa nzeru.


Udzu unyala, duwa lifota, koma mau a Mulungu wathu adzakhala nthawi zachikhalire.


Tukulani maso anu kumwamba, ndipo muyang'ane pansi padziko pakuti kumwamba kudzachoka ngati utsi, ndi dziko lidzatha ngati chofunda, ndipo iwo amene akhala m'menemo adzafa ngati njenjete; koma chipulumutso changa chidzakhala kunthawi zonse, ndi chilungamo changa sichidzachotsedwa.


Koma mau anga ndi malemba anga, amene ndinalamulira atumiki anga aneneriwo, kodi sanawapeze makolo anu? Ndipo anabwera, nati, Monga umo Yehova wa makamu analingirira kutichitira ife, monga mwa njira zathu ndi monga mwa machitidwe athu, momwemo anatichitira.


Mulungu sindiye munthu, kuti aname; kapena mwana wa munthu, kuti aleke; kodi anena, osachita?


Thambo ndi dziko lapansi zidzachoka, koma mau anga sadzachoka ai.


Pakuti indetu ndinena kwa inu, Kufikira litapitirira thambo ndi dziko, kalemba kakang'ono kamodzi kapena kansonga kake kamodzi sikadzachokera kuchilamulo, kufikira zitachitidwa zonse.


Indetu ndinena ndi inu, Mbadwo uno sudzapita kufikira zinthu izi zonse zitachitika.


Koma za tsiku ilo, kapena nthawi yake sadziwa munthu, angakhale angelo mu Mwamba, angakhale Mwana, koma Atate ndiye.


Thambo ndi dziko lapansi zidzapita; koma mau anga sadzapita.


ngati tikhala osakhulupirika, Iyeyu akhala wokhulupirika; pakuti sangathe kudzikana yekha.


m'chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu, wosanamayo, analonjeza zisanayambe nthawi zosayamba;


Ndipo ndinaona, mpando wachifumu waukulu woyera, ndi Iye wakukhalapo, amene dziko ndi m'mwamba zinathawa pamaso pake, ndipo sanapezedwe malo ao.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa