Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Marko 12:31 - Buku Lopatulika

31 Lachiwiri ndi ili, Uzikonda mnzako monga udzikonda mwini. Palibe lamulo lina lakuposa awa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

31 Lachiwiri ndi ili, Uzikonda mnzako monga udzikonda mwini. Palibe lamulo lina lakuposa awa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

31 Lamulo lachiŵiri lake ndi ili, ‘Uzikonda mnzako monga momwe umadzikondera iwe wemwe.’ Palibe lamulo lina loposa malamulo ameneŵa.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

31 Lachiwiri ndi ili: ‘Konda mnansi wako monga iwe mwini.’ Palibe lamulo lina loposa amenewa.”

Onani mutuwo Koperani




Marko 12:31
15 Mawu Ofanana  

Usamasautsa mnansi wako, kapena kulanda zake; mphotho yake ya wolipidwa isakhale ndi iwe kufikira m'mawa.


Usamabwezera chilango, kapena kusunga kanthu kukhosi pa ana a anthu a mtundu wako; koma uzikonda mnansi wako monga udzikonda wekha; Ine ndine Yehova.


Ndipo lachiwiri lolingana nalo ndili, Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe mwini.


Chifukwa chake zinthu zilizonse mukafuna kuti anthu achitire inu, inunso muwachitire iwo zotero; pakuti icho ndicho chilamulo ndi aneneri.


Ndipo mlembiyo anati kwa Iye, Chabwino, Mphunzitsi, mwanena zoona kuti ndiye mmodzi; ndipo palibe wina, koma Iye:


Ndipo iye anayankha nati, Uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu yako yonse, ndi nzeru zako zonse, ndi mnansi wako monga iwe mwini.


Pakuti mau amodzi akwaniritsa chilamulo chonse ndiwo; Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe mwini.


Ndipo lamulo ili tili nalo lochokera kwa Iye, kuti iye amene akonda Mulungu akondenso mbale wake.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa