Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Marko 10:50 - Buku Lopatulika

50 Ndipo iye anataya chofunda chake, nazunzuka, nadza kwa Yesu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

50 Ndipo iye anataya chofunda chake, nazunzuka, nadza kwa Yesu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

50 Pomwepo iye uja adadzambatuka, mwinjiro wake uko chi, kuthamangira kwa Yesu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

50 Anaponya mkanjo wake kumbali, analumpha nabwera kwa Yesu.

Onani mutuwo Koperani




Marko 10:50
5 Mawu Ofanana  

Ndipo pamene Yesu analikuyenda m'mbali mwa nyanja ya Galileya, anaona abale awiri, Simoni wonenedwa Petro, ndi Andrea, mbale wake, analikuponya khoka m'nyanja; popeza anali asodzi a nsomba.


Ndipo Yesu anaima, nati, Mwitaneni. Ndipo anaitana wakhunguyo, nanena naye, Limba mtima; nyamuka, akuitana.


Ndipo Yesu anamyankha, nati, Ufuna kuti ndikuchitire chiyani? Ndipo wakhunguyo anati kwa Iye, Raboni, ndilandire kuona kwanga.


Chifukwa chake ifenso, popeza tizingidwa nao mtambo waukulu wotere wa mboni, titaye cholemetsa chilichonse, ndi tchimoli limangotizinga, ndipo tithamange mwachipiriro makaniwo adatiikira, ndi kupenyerera woyambira ndi womaliza wa chikhulupiriro chathu,


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa