Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Maliro 5:6 - Buku Lopatulika

6 Tinagwira mwendo Ejipito ndi Asiriya kuti tikhute zakudya.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 Tinagwira mwendo Ejipito ndi Asiriya kuti tikhute zakudya.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 Tidachita chibwenzi ndi Aejipito ndiponso ndi Aasiriya, kuti mwina iwo nkutipatsako chakudya.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.

Onani mutuwo Koperani




Maliro 5:6
15 Mawu Ofanana  

Ndipo Abrahamu anati kwa mnyamata wake wamkulu wa pa nyumba yake, amene analamulira pa zonse anali nazo, Taikatu dzanja lako pansi pa ntchafu yanga:


Atachoka pamenepo, anakomana naye Yehonadabu mwana wa Rekabu wakudzamchingamira; namlonjera, nanena naye, Mtima wako ngwoongoka kodi, monga mtima wanga uvomerezana nao mtima wako? Nati Yehonadabu, Momwemo. Ukatero undipatse dzanja lako. Nampatsa dzanja lake, namkweretsa pali iye pagaleta.


Ndipo unanka kwa mfumu, utadzola mafuta ndi kuchulukitsa zonunkhira zako; ndipo unatumiza atumwi ako kutali; ndipo wadzichepetsa wekha kufikira kunsi kumanda.


Tsopano uli nacho chiyani m'njira ya ku Ejipito, kumwa madzi a mtsinje wa Nailo? Uli nacho chiyani m'njira ya ku Asiriya, kumwa madzi a mtsinje wa Yufurate?


Bwanji uyendayenda kwambiri ndi kusintha njira yako? Udzachitanso manyazi ndi Ejipito monga unachita manyazi ndi Asiriya.


Mumfuulire iye pomzungulira iye; pakuti wagwira mwendo; malinga ake agwa; makoma ake agwetsedwa; pakuti ndi kubwezera chilango kwa Yehova; mumbwezere chilango; monga iye wachita mumchitire iye momwemo.


Maso athu athedwa, tikali ndi moyo, poyembekeza thandizo chabe; kudikira tinadikira mtundu wosatha kupulumutsa.


Pakuti anapepula lumbiro, ndi kuthyola pangano, angakhale anapereka dzanja lake; popeza anachita izi zonse sadzapulumuka.


Efuremu akudya mphepo, natsata mphepo ya kum'mawa; tsiku lonse achulukitsa mabodza ndi chipasuko, ndipo achita pangano ndi Asiriya, natenga mafuta kunka nao ku Ejipito.


Pamene Efuremu anaona nthenda yake, ndi Yuda bala lake, Efuremu anamuka kwa Asiriya, natumiza kwa mfumu Yarebu; koma iye sakhoza kukuchiritsani, kapena kupoletsa bala lanu.


Ndipo Efuremu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru; aitanira kwa Ejipito, amuka kwa Asiriya.


Sadzakhala m'dziko la Yehova; koma Efuremu adzabwerera kunka ku Ejipito; ndipo adzadya chakudya chodetsa mu Asiriya.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa