Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Maliro 5:5 - Buku Lopatulika

5 Otilondola atigwira pakhosi pathu, tatopa osaona popumira.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

5 Otilondola atigwira pakhosi pathu, tatopa osaona popumira.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

5 Amatikankha mwankhanza, goli lili m'khosi mwathu. Ngakhale titope, satilola kupumula.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

5 Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.

Onani mutuwo Koperani




Maliro 5:5
14 Mawu Ofanana  

Yehova atero kwa ine: Udzipangire zomangira ndi magoli, nuziike pakhosi pako;


Ndipo padzakhala, kuti mtundu ndi ufumu umene sudzamtumikira Nebukadinezara yemweyo mfumu ya ku Babiloni, mtundu umenewo Ine ndidzalanga, ati Yehova, ndi lupanga, ndi njala, ndi mliri, mpaka nditatha onse ndi dzanja lake.


Pakuti atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israele: Ndaika goli lachitsulo pa khosi la amitundu onsewa, kuti amtumikire Nebukadinezara mfumu ya ku Babiloni; ndipo adzamtumikira iye; ndipo ndampatsanso nyama zakuthengo.


Yehova wa makamu atero: Makoma otakata a Babiloni adzagwetsedwa ndithu, ndi zitseko zake zazitali zidzatenthedwa ndi moto; anthu adzagwirira ntchito chabe, ndi mitundu ya anthu idzagwirira moto, nidzatopa.


Goli la zolakwa zanga lamangidwa ndi dzanja lake; zalukidwa, zakwera pakhosi panga; iye wakhumudwitsa mphamvu yanga; Ambuye wandipereka m'manja mwao, sindithai kuwagonjetsa.


Yuda watengedwa ndende chifukwa cha msauko ndi ukapolo waukulu; akhala mwa amitundu, sapeza popuma; onse akumlondola anampeza pakati popsinjikiza.


Otilondola anaposa ziombankhanga za m'mlengalenga m'liwiro lao, anatithamangitsa pamapiri natilalira m'chipululu.


Chifukwa chake atero Yehova, Taonani, ndilingirira choipa pa banja ili, chimene simudzachotsako makosi anu, kapena kuyenda modzikuza inu; pakuti nyengo iyi ndi yoipa.


Senzani goli langa, ndipo phunzirani kwa Ine; chifukwa ndili wofatsa ndi wodzichepetsa mtima: ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu.


Nanga bwanji tsopano mulikumuyesa Mulungu, kuti muike pa khosi la ophunzira goli, limene sanathe kunyamula kapena makolo athu kapena ife?


chifukwa chake mudzatumikira adani anu amene Yehova adzakutumizirani, ndi njala, ndi ludzu, ndi usiwa, ndi kusowa zinthu zonse; ndipo adzaika goli lachitsulo pakhosi panu, kufikira atakuonongani.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa