Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Maliro 5:1 - Buku Lopatulika

1 Yehova, kumbukirani chotigwerachi, penyani nimuone chitonzo chathu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Yehova, kumbukirani chotigwerachi, penyani nimuone chitonzo chathu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Inu Chauta, kumbukirani zimene zatigwera. Muyang'ane, muwone m'mene anthu akutinyozera.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.

Onani mutuwo Koperani




Maliro 5:1
26 Mawu Ofanana  

Nanena nane iwo, Otsalawo otsala andende uko kudzikoko akulukutika kwakukulu, nanyozedwa; ndi linga la Yerusalemu lapasuka, ndi zipata zake zatenthedwa ndi moto.


Mukumbukire mau mudalamulira mtumiki wanu Mose, ndi kuti, Mukalakwa, ndidzakubalalitsani mwa mitundu ya anthu;


Imvani, Mulungu wathu, popeza tanyozeka ife; muwabwezere chitonzo chao pamtu pao, ndi kuwapereka akhale chofunkhidwa m'dziko la ndende;


Mukumbukire kuti mwandiumba ngati dothi; ndipo kodi mudzandibwezera kufumbi?


Kumbukira kuti moyo wanga ndiwo mphepo, diso langa silidzaonanso chokoma.


Penyani kuzunzika kwanga, nimundilanditse; pakuti sindiiwala chilamulo chanu.


Mukumbukire ichi, Yehova, mdaniyo anatonza, ndipo anthu opusa ananyoza dzina lanu.


Ndipo anansi athu amene anatonza Inu muwabwezere chotonza chao, kasanu ndi kawiri kumtima kwao, Ambuye.


Takhala chotonza cha anansi athu, ndi choseketsa ndi cholalatitsa iwo akutizinga.


Ndaika alonda pa malinga ako, Yerusalemu; iwo sadzakhala chete usana pena usiku; inu akukumbutsa Yehova musakhale chete,


Inu Yehova, mudziwa; mundikumbukire ine, mundiyang'anire Ine, mundibwezere chilango pa ondisautsa ine; musandichotse m'chipiriro chanu; dziwani kuti chifukwa cha Inu ndanyozedwa.


Tili ndi manyazi, chifukwa tamva mnyozo; manyazi aphimba nkhope zathu; pakuti alendo alowa m'malo opatulika a nyumba ya Yehova.


Anthu ake onse ausa moyo nafunafuna mkate; ndi zokondweretsa zao agula zakudya kuti atsitsimutse moyo wao; taonani, Yehova, nimupenye; pakuti ndasanduka wonyansa.


Onani, Yehova; pakuti ndavutika, m'kati mwanga mugwedezeka; mtima wanga wasanduka mwa ine; pakuti ndapikisana nanu ndithu; kunjako lupanga limangopha ana; m'nyumba muli imfa.


Udyo wake unali m'nsalu zake; sunakumbukire chitsiriziro chake; chifukwa chake watsika mozizwitsa; ulibe wakuutonthoza; taonani, Yehova, msauko wanga, pakuti mdaniyo wadzikuza yekha.


Onse opita panjira akuombera manja: Atsonya, napukusira mitu yao pa mwana wamkazi wa Yerusalemu, nati, kodi uwu ndi mzinda wotchedwa wokongola, wangwiro, wokondweretsa dziko lonse?


Onani Yehova, nimupenye, mwachitira ayani ichi? Kodi akazi adzadya zipatso zao, kunena ana amene anawalera wokha? Kodi wansembe ndi mneneri adzaphedwa m'malo opatulika a Ambuye?


Kumbukirani msauko wanga ndi kusochera kwanga, ndizo chivumulo ndi ndulu.


kufikira Yehova adzazolika kumwamba ndi kuona.


Mwamva chitonzo chao, Yehova, ndi zopangira zao zonse za pa ine,


Yehova, ndinamva mbiri yanu ndi mantha; Yehova, tsitsimutsani ntchito yanu pakati pa zaka, pakati pa zaka mudziwitse; pa mkwiyo mukumbukire chifundo.


Ndipo ananena, Yesu, ndikumbukireni m'mene mulowa Ufumu wanu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa