Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Maliro 3:11 - Buku Lopatulika

11 Wapambutsa njira zanga, nanding'amba; nandipululutsa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

11 Wapambutsa njira zanga, nanding'amba; nandipululutsa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

11 Adandisiyitsa njira nanding'ambang'amba, kenaka nkundisiya.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

11 Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.

Onani mutuwo Koperani




Maliro 3:11
20 Mawu Ofanana  

Koma tsopano wandilemetsa Iye; mwapasula msonkhano wanga wonse.


Potero mzimu wanga wakomoka mwa ine; mtima wanga utenga nkhawa m'kati mwanga.


Dziwitsani ichi inu oiwala Mulungu, kuti ndingakumwetuleni, ndipo mungasowepo mpulumutsi.


Ndipo zipata zake zidzalira maliro; ndipo iye adzakhala bwinja, nadzakhala pansi.


Ndipo ndidzaika pa iwo mitundu inai, ati Yehova, lupanga lakupha, agalu akung'amba, mbalame za m'mlengalenga, ndi zilombo zapansi, zakulusa ndi kuononga.


Ndipo ndidzayesa mzindawu chodabwitsa, ndi chotsonyetsa; onse amene adzapitapo adzadabwa ndi kutsonya chifukwa cha zopanda pake zonse.


Ndipo minda idzagulidwa m'dziko lino, limene muti, Ndilo bwinja, lopanda munthu kapena nyama; loperekedwa m'dzanja la Ababiloni.


Chifukwa chake mkango wotuluka m'nkhalango udzawapha, ndi mmbulu wa madzulo udzawafunkha, nyalugwe adzakhalira m'mizinda mwao, onse amene atulukamo adzamwetulidwa; pakuti zolakwa zili zambiri, ndi mabwerero ao achuluka.


Ulangizidwe, Yerusalemu, ungakuchokere moyo wanga, ndingakuyese iwe bwinja, dziko losakhalamo anthu.


Anatumiza moto wochokera kumwamba kulowa m'mafupa anga, unawagonjetsa; watchera mapazi anga ukonde, wandibwezera m'mbuyo; wandipululutsa ndi kundilefula tsiku lonse.


Andikhalira chilombo cholalira kapena mkango mobisalira.


Anatero, chilombo chachinai ndicho ufumu wachinai padziko lapansi, umene udzasiyana nao maufumu onse, nudzalusira dziko lonse lapansi, nudzalipondereza ndi kuliphwanya.


Tiyeni, tibwerere kunka kwa Yehova; pakuti wang'amba, nadzatipoletsera; wakantha, nadzatimanga.


Ndipo otsala a Yakobo adzakhala mwa amitundu, pakati pa mitundu yambiri ya anthu, ngati mkango mwa nyama zakuthengo, ngati msona wa mkango mwa magulu a nkhosa; umenewo ukapitako, upondereza, numwetula, ndipo palibe wakupulumutsa.


Onani, nyumba yanu yasiyidwa kwa inu yabwinja.


Ndipo anathira fumbi pamitu pao, nafuula, ndi kulira, ndi kuchita maliro, nanena, Tsoka, tsoka, mzinda waukuluwo, umene analemerezedwa nao onse akukhala nazo zombo panyanja, chifukwa cha kulemera kwake, pakuti mu ora limodzi unasanduka bwinja.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa