Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Malaki 3:14 - Buku Lopatulika

14 Mwanena, Kutumikira Mulungu nkwa chabe; ndipo tapindulanji ndi kusunga udikiro wake, ndi kuyenda ovala zamaliro pamaso pa Yehova wa makamu?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

14 Mwanena, Kutumikira Mulungu nkwa chabe; ndipo tapindulanji ndi kusunga udikiro wake, ndi kuyenda ovala zamaliro pamaso pa Yehova wa makamu?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

14 Mwanena kuti, ‘Kutumikira Mulungu nkwachabe. Kodi pali phindu lanji kumatsata malamulo a Chauta Wamphamvuzonse, kapena kumaonetsa chisoni pamaso pake?

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

14 “Mwanena kuti, ‘Kutumikira Mulungu nʼkosapindulitsa. Kodi timapindulanji pochita zofuna zake, ndi kumayenda ngati anamfedwa pamaso pa Yehova Wamphamvuzonse?

Onani mutuwo Koperani




Malaki 3:14
16 Mawu Ofanana  

amene anati kwa Mulungu, Tichokereni; ndipo, Angatichitire chiyani Wamphamvuyonse?


Pakuti anati, Munthu sapindula kanthu nako kuvomerezana naye Mulungu.


pakuti munena, Upindulanji nacho? Posachimwa ndinapindula chiyani chimene sindikadapindula pochimwa?


Komabe iwe sunandiitane Ine, Yakobo; koma iwe walema ndi Ine, Israele.


Amati, Bwanji ife tasala kudya, ndipo Inu simuona? Ndi bwanji ife tavutitsa moyo wathu, ndipo Inu simusamalira? Taonani, tsiku la kusala kudya kwanu inu mupeza kukondwerera kwanu, ndi kutsendereza antchito anu onse.


Koma iwo ati, Palibe chiyembekezero; pakuti ife tidzatsata zilingaliro zathu, ndipo tidzachita yense monga mwa kuuma kwa mtima wake woipa.


Kaniza phazi lako lisakhale losavala nsapato, ndi m'mero mwako musakhale ndi ludzu; koma unati, Palibe chiyembekezo, iai; pakuti ndakonda alendo, ndipo ndidzatsata pambuyo pao.


Koma chilekere ife kufukizira mfumu yaikazi ya kumwamba, ndi kumthirira iye nsembe zothira, tasowa zonse, tathedwa ndi lupanga ndi njala.


Abwerera, koma si kwa Wam'mwambayo; akunga uta wosakhulupirika; akalonga ao adzagwa ndi lupanga mwa chipongwe cha lilime lao; ichi ndicho adzawasekera m'dziko la Ejipito.


Koma ngakhale tsopano, ati Yehova, munditembenukire Ine ndi mtima wanu wonse, ndi kusala, ndi kulira, ndi kuchita maliro;


Ndipo kudzachitika nthawi yomweyi kuti ndidzasanthula Yerusalemu ndi nyali, ndipo ndidzalanga amunawo okhala ndi nsenga, onena m'mtima mwao, Yehova sachita chokoma, kapena kuchita choipa.


Mau anu andilimbira, ati Yehova. Koma inu mukuti, Tanena motsutsana nanu ndi chiyani?


Khalani osautsidwa, lirani, lirani misozi; kuseka kwanu kusanduke kulira, ndi chimwemwe chanu chisanduke chisoni.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa