Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Machitidwe a Atumwi 7:15 - Buku Lopatulika

15 Ndipo Yakobo anatsikira ku Ejipito; ndipo anamwalira, iye ndi makolo athu;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

15 Ndipo Yakobo anatsikira ku Ejipito; ndipo anamwalira, iye ndi makolo athu;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

15 Motero Yakobe adapita ku Ejipito, iye ndi makolo athu omwe aja. Onsewo adakamwalira kumeneko.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

15 Motero Yakobo anapita ku Igupto, kumene iye ndiponso makolo athu anamwalira.

Onani mutuwo Koperani




Machitidwe a Atumwi 7:15
13 Mawu Ofanana  

Ndipo Israele anamuka ulendo wake ndi zonse anali nazo, nafika ku Beereseba, napereka nsembe kwa Mulungu wa Isaki atate wake.


koma pamene ndidzagona ndi makolo anga, udzanditenge ine kutuluka m'dziko la Ejipito, ukandiike ine m'manda mwao. Ndipo iye anati, Ndidzachita monga mwanena.


Pamene Yakobo anatha kulangiza ana ake aamuna, anafunya mapazi ake pakama, natsirizika, nasonkhanitsidwa kwa anthu a mtundu wake.


Pamenepo Israele analowa mu Ejipito; ndi Yakobo anakhala mlendo m'dziko la Hamu.


Ndipo anafa Yosefe, ndi abale ake onse, ndi mbadwo uwo wonse.


Ndipo Mose anamuka nao mafupa a Yosefe; pakuti adawalumbiritsatu ana a Israele ndi kuti, Mulungu adzakuzondani ndithu ndipo mukakwere nao mafupa anga osawasiya kuno.


kuti makolo athu anatsikira kunka ku Ejipito, ndipo tinakhala mu Ejipito masiku ambiri; ndipo Aejipito anachitira zoipa ife, ndi makolo athu.


Makolo anu anatsikira ku Ejipito ndiwo anthu makumi asanu ndi awiri; ndipo Yehova Mulungu wanu anakusandulizani tsopano muchuluke ngati nyenyezi za kumwamba.


Ndipo muyankhe ndi kuti pamaso pa Yehova Mulungu wanu, Kholo langa ndiye Mwaramu wakuti atayike, natsika kunka ku Ejipito, nagoneragonera komweko ali nao anthu pang'ono, nasandukako mtundu waukulu, wamphamvu, ndi wochuluka anthu ake;


Ndipo mafupa a Yosefe amene ana a Israele anakwera nao kuchokera ku Ejipito anawaika ku Sekemu, pa kadziko kamene adakagula Yakobo kwa ana a Hamori atate wa Sekemu ndi kuwapatsa ndalama zana; ndipo anakhala cholowa cha ana a Yosefe.


Ndi kwa Isaki ndinapatsa Yakobo ndi Esau, ndipo ndinampatsa Esau phiri la Seiri likhale lakelake; koma Yakobo ndi ana ake anatsikira kunka ku Ejipito.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa