Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Machitidwe a Atumwi 21:30 - Buku Lopatulika

30 Ndipo mzinda wonse unasokonezeka, ndipo anthu anathamangira pamodzi; nagwira Paulo namkoka kumtulutsa mu Kachisi; ndipo pomwepo pamakomo panatsekedwa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

30 Ndipo mudzi wonse unasokonezeka, ndipo anthu anathamangira pamodzi; nagwira Paulo namkoka kumtulutsa m'Kachisi; ndipo pomwepo pamakomo panatsekedwa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

30 Tsono mumzinda monse mudaloŵa chisokonezo ndipo anthu onse adathamangira pamodzi namgwira Pauloyo. Adamkokera kunja kwa Nyumba ya Mulungu, nkutseka pa makomo nthaŵi yomweyo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

30 Mzinda wonse unasokonezeka, ndipo anthu anabwera akuthamanga kuchokera kumbali zonse. Anamugwira Paulo, namukokera kunja kwa Nyumbayo, ndipo nthawi yomweyo anatseka zipata.

Onani mutuwo Koperani




Machitidwe a Atumwi 21:30
9 Mawu Ofanana  

Koma Yehoyada wansembe analamulira atsogoleri a mazana oyang'anira khamu, nanena nao, Mumtulutse mkaziyo pabwalo pakati pa mipambo; womtsata iye mumuphe ndi lupanga; pakuti wansembe adati, Asaphedwe m'nyumba ya Yehova.


Ndipo Herode mfumuyo pakumva ichi anavutika, ndi Yerusalemu yense pamodzi naye.


Ndipo m'mene adalowa mu Yerusalemu mzinda wonse unasokonezeka, nanena, Ndani uyu?


nanyamuka namtulutsira Iye kunja kwa mzindawo, nanka naye pamutu paphiri pamene panamangidwa mzinda wao, kuti akamponye Iye pansi.


Ndipo m'mzinda monse munachita piringupiringu, nathamangira onse pamodzi ku bwalo losewera, atagwira Gayo ndi Aristariko, anthu a ku Masedoniya, alendo anzake a Paulo.


Chifukwa cha izi Ayuda anandigwira mu Kachisi, nayesa kundipha.


paulendo kawirikawiri, moopsa mwake mwa mitsinje, moopsa mwake mwa olanda, moopsa modzera kwa mtundu wanga, moopsa modzera kwa amitundu, moopsa m'mzinda, moopsa m'chipululu, moopsa m'nyanja, moopsa mwa abale onyenga;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa