Machitidwe a Atumwi 18:18 - Buku Lopatulika18 Paulo atakhala chikhalire masiku ambiri, anatsazika abale, nachoka pamenepo, napita m'ngalawa ku Siriya, pamodzi naye Prisila ndi Akwila; popeza anameta mutu wake mu Kenkrea; pakuti adawinda. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 201418 Paulo atakhala chikhalire masiku ambiri, anatsazika abale, nachoka pamenepo, napita m'ngalawa ku Siriya, pamodzi naye Prisila ndi Akwila; popeza anameta mutu wake m'Kenkrea; pakuti adawinda. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa18 Paulo adakhalabe ku Korinto masiku ambiri. Pambuyo pake adalaŵirana ndi abale, naloŵa m'chombo kupita ku Siriya pamodzi ndi Prisila ndi Akwila. Asanaloŵe m'chombomo, Paulo adameta tsitsi lake ku Kenkrea, chifukwa anali atachita lumbiro kwa Mulungu. Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero18 Paulo anakhalabe ku Korinto masiku ambiri. Kenaka anawasiya abale nakwera sitima ya pamadzi kupita ku Siriya, pamodzi ndi Prisila ndi Akula. Asanakakwere sitima ya pamadzi, anameta tsitsi lake ku Kenkreya chifukwa anali atalumbira. Onani mutuwo |