Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Machitidwe a Atumwi 14:18 - Buku Lopatulika

18 Pakunena izo, anavutika pakuletsa makamu kuti asapereke nsembe kwa iwo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

18 Pakunena izo, anavutika pakuletsa makamu kuti asapereke nsembe kwa iwo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

18 Ngakhale ndi mau ameneŵa, adavutika kuŵaletsa anthu aja kuti asaŵaphere nsembe.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

18 Ngakhale ndi mawu awa, anavutika kuletsa gulu la anthu kuti asapereke nsembe kwa iwo.

Onani mutuwo Koperani




Machitidwe a Atumwi 14:18
8 Mawu Ofanana  

Ndipo Yehova anati, Taonani, anthu ali amodzi, ndipo onse ali nacho chinenedwe chao chimodzi; ndipo ichi ayamba kuchita: ndipo tsopano palibe kanthu kakuletsedwa nao kamene akafuna kuchita.


Ndipo anati iwo, Baima; natinso, Uyu anadza kuno kukhala ngati mlendo, ndipo afuna kutilamulira; tsopano tidzakuchitira iwe koipa koposa iwo. Ndipo iwo anamkakamiza munthuyo Loti ndithu, nayandikira kuti aswe chitseko.


Chifukwa unalemera mtima wa anthu awa, ndipo m'makutu ao anamva mogontha, ndipo maso ao anatsinzina; kuti asaone konse ndi maso, asamve ndi makutu, asazindikire ndi mtima wao, asatembenuke, ndipo ndisawachiritse iwo.


Pamenepo Yesu, pozindikira kuti alikufuna kudza kudzamgwira Iye, kuti amlonge ufumu, anachokanso kunka kuphiri pa yekha.


Koma sanadzisiyire Iye mwini wopanda umboni, popeza anachita zabwino, nakupatsani inu zochokera kumwamba mvula ndi nyengo za zipatso, ndi kudzaza mitima yanu ndi chakudya ndi chikondwero.


Ndipo anafika kumeneko Ayuda kuchokera ku Antiokeya ndi Ikonio; nakopa makamu, ndipo anamponya Paulo miyala, namguzira kunja kwa mzinda; namuyesa kuti wafa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa