Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Luka 22:62 - Buku Lopatulika

62 Ndipo anatuluka, nalira misozi ndi kuwawa mtima.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

62 Ndipo anatuluka, nalira misozi ndi kuwawa mtima.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

62 Pamenepo adatuluka, nakalira kwambiri chifukwa cha chisoni chachikulu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

62 Ndipo iye anapita panja nakalira kwambiri.

Onani mutuwo Koperani




Luka 22:62
14 Mawu Ofanana  

Pakuti ndidzafotokozera mphulupulu yanga; nditenga nkhawa chifukwa cha tchimo langa.


Kumva ndamva Efuremu alinkulirira kotero, Mwandilanga ine, ndipo ndalangidwa, monga mwanawang'ombe wosazolowera goli; munditembenuze ine, ndipo ine ndidzatembenuka; pakuti inu ndinu Yehova Mulungu wanga.


Ndipo akupulumuka mwa iwo adzapulumuka, koma adzakhala kumapiri ngati njiwa za kuzigwa, onse akubuula, aliyense m'mphulupulu zake.


Ndipo ndidzatsanulira pa nyumba ya Davide, ndi pa okhala mu Yerusalemu, mzimu wa chisomo ndi wakupembedza; ndipo adzandipenyera Ine amene anandipyoza; nadzamlira ngati munthu alira mwana wake mmodzi yekha, nadzammvera zowawa mtima, monga munthu amvera zowawa mtima mwana wake woyamba.


Ndipo Petro anakumbukira mau amene Yesu adati, Asanalire tambala udzandikana katatu. Ndipo anatulukira kunja, nalira ndi kuwawa mtima.


Odala ali achisoni; chifukwa adzasangalatsidwa.


Ndipo pomwepo tambala analira kachiwiri. Ndipo Petro anakumbukira umo Yesu anati kwa iye, kuti, Tambala asanalire kawiri udzandikana katatu. Ndipo pakuganizira ichi analira misozi.


Ndipo Ambuye anapotoloka, nayang'ana Petro. Ndipo Petro anakumbukira mau a Ambuye, kuti anati kwa iye, Asanalire tambala lero lino, udzandikana Ine katatu.


Ndipo amuna amene analikusunga Yesu anamnyoza Iye, nampanda.


Chifukwa chake iye wakuyesa kuti ali chilili, ayang'anire kuti angagwe.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa