Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Luka 18:38 - Buku Lopatulika

38 Ndipo anafuula, nanena, Yesu, Mwana wa Davide, mundichitire chifundo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

38 Ndipo anafuula, nanena, Yesu, Mwana wa Davide, mundichitire chifundo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

38 Apo iye adanena mokweza mau kuti, “Inu Yesu, Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

38 Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”

Onani mutuwo Koperani




Luka 18:38
14 Mawu Ofanana  

Chifundonso ndi chanu, Ambuye, Chifukwa Inu mubwezera munthu aliyense monga mwa ntchito yake.


Ndipo padzatuluka mphukira pa tsinde la Yese, ndi nthambi yotuluka m'mizu yake idzabala zipatso;


Taonani, masiku alinkudza, ati Yehova, ndidzamuukitsira Davide Mphukira wolungama, ndipo Iye adzakhala Mfumu, adzachita mwanzeru, nadzachita chiweruzo ndi chilungamo m'dziko lino.


Ndipo makamu onse a anthu anazizwa, nanena, Uyu si mwana wa Davide kodi?


Ndipo onani, mkazi wa ku Kanani anatuluka m'malire, nafuula, nati, Mundichitire ine chifundo Ambuye, mwana wa Davide; mwana wanga wamkazi wagwidwa koopsa ndi chiwanda.


Koma ansembe aakulu ndi alembi, m'mene anaona zozizwitsa zomwe Iye anazichita, ndi ana alinkufuula ku Kachisiko kuti, Hosana kwa Mwana wa Davide, anapsa mtima,


Ndipo mipingo yakumtsogolera ndi yakumtsatira, inafuula, kuti, Hosana kwa Mwana wa Davide! Wolemekezeka ndiye wakudza m'dzina la Ambuye! Hosana mu Kumwambamwamba!


Ndipo popita Yesu kuchokera kumeneko, anamtsata Iye anthu awiri akhungu, ofuula ndi kuti, Mutichitire ife chifundo, mwana wa Davide.


Ndipo anamuuza iye, kuti, Yesu Mnazarayo alinkupita.


Ndipo iwo akutsogolera anamdzudzula iye, kuti akhale chete; koma iye anafuulitsa chifuulire, Mwana wa Davide, mundichitire chifundo.


wakunena za Mwana wake, amene anabadwa, wa mbeu ya Davide, monga mwa thupi,


Ine Yesu ndatuma mngelo wanga kukuchitirani umboni za izi mu Mipingo. Ine ndine muzu ndi mbadwa ya Davide, nyenyezi yonyezimira ya nthanda.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa