Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Luka 12:46 - Buku Lopatulika

46 mbuye wa kapolo uyo adzafika tsiku lakuti samuyembekezera, ndi nthawi yakuti saidziwa, nadzamdula iye pakati nadzamuika dera lake pamodzi ndi anthu osakhulupirira.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

46 mbuye wa kapolo uyo adzafika tsiku lakuti samuyembekezera, ndi nthawi yakuti saidziwa, nadzamdula iye pakati nadzamuika dera lake pamodzi ndi anthu osakhulupirira.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

46 Tsono mbuye wake adzangoti mbwe mwadzidzidzi, pa tsiku limene iye sakumuyembekeza. Choncho adzamlanga koopsa, ndipo adzamtaya ku malo a anthu osakhulupirika.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

46 Mbuye wake adzabwera tsiku limene iye sakumuyembekezera ndi ora limene iye sakudziwa. Iye adzamulanga ndi kumusiya kumalo kumene kuli osakhulupirira.

Onani mutuwo Koperani




Luka 12:46
14 Mawu Ofanana  

Ili ndi gawo la munthu woipa, lochokera kwa Mulungu, ndi cholowa amuikiratu Mulungu.


Yehova ayesa wolungama mtima, koma moyo wake umuda woipa ndi iye wakukonda chiwawa.


Pakuti ochita zoipa adzadulidwa; koma iwo akuyembekeza Yehova, iwowa adzalandira dziko lapansi.


Pakuti Yehova sadzasiya anthu ake, ndipo sadzataya cholowa chake.


mbuye wa kapoloyo adzafika tsiku losamuyembekeza iye, ndi nthawi yosadziwa iye,


nadzamdula, nadzaika pokhala pake ndi anthu onyenga; pomwepo padzakhala kulira ndi kukukuta mano.


Khalani okonzeka inunso; chifukwa nthawi imene simulingirira, Mwana wa Munthu akudza.


Koma kapolo uyo akanena mumtima mwake, Mbuye wanga azengereza kudza; ndimo akayamba kupanda anyamata ndi adzakazi ndi kudya ndi kumwa, ndi kuledzera;


Ndipo kapolo uyo, wodziwa chifuniro cha mbuye wake, ndipo sanakonze, ndi kusachita zonga za chifuniro chakecho, adzakwapulidwa mikwapulo yambiri.


(Taonani, ndidza ngati mbala. Wodala iye amene adikira, nasunga zovala zake, kuti angayende wausiwa, nangapenye anthu usiwa wake.)


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa