Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Levitiko 7:26 - Buku Lopatulika

26 Ndipo musamadya mwazi uliwonse, kapena wa mbalame, kapena wa nyama, m'nyumba zanu zonse.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

26 Ndipo musamadya mwazi uliwonse, kapena wa mbalame, kapena wa nyama, m'nyumba zanu zonse.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

26 Ndiponso kulikonse kumene akakhale, asadye magazi aliwonse, ambalame kapena anyama.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

26 Ndipo kulikonse kumene mukakhale musakadye magazi a mbalame iliyonse kapena magazi a nyama iliyonse.

Onani mutuwo Koperani




Levitiko 7:26
17 Mawu Ofanana  

Koma nyama, m'mene muli moyo wake, ndiwo mwazi wake, musadye.


Uzitero nazo ng'ombe zako, ndi nkhosa zako; masiku asanu ndi atatu akhale ndi amai wake; tsiku lachisanu ndi chitatu uzimpereka kwa Ine.


Chifukwa chake unene nao, Atero Ambuye Yehova, Mumadyera kumodzi ndi mwazi, mumakwezera maso anu kumafano anu, ndi kukhetsa mwazi; ndipo kodi mudzakhala nalo dziko cholowa chanu?


Musamadya kanthu ndi mwazi wake; musamachita nyanga, kapena kuombeza ula.


Likhale lemba losatha m'mibadwo yanu m'nyumba zanu zonse, musamadya kapena mafuta kapena mwazi.


Pakuti aliyense akadya mafuta a nyama imene amabwera nayo ikhale nsembe yamoto ya kwa Yehova, munthu amene akadya awa achotsedwe kwa anthu a mtundu wake.


Aliyense akadya mwazi uliwonse, munthuyo achotsedwe kwa anthu a mtundu wake.


Chifukwa chake Yesu anati kwa iwo, Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Ngati simukudya thupi la Mwana wa Munthu ndi kumwa mwazi wake, mulibe moyo mwa inu nokha.


koma kuti tilembere kwa iwo, kuti asale zonyansa za mafano, ndi dama, ndi zopotola, ndi mwazi.


kuti musale nsembe za mafano, ndi mwazi, ndi zopotola, ndi dama; ngati mudzisungitsa pa zimenezi, kudzakhala bwino kwa inu. Tsalani bwino.


Tili ndi maomboledwe mwa mwazi wake, chikhululukiro cha zochimwa, monga mwa kulemera kwa chisomo chake,


Mwazi wao wokha musamadya; muziuthira panthaka ngati madzi.


Koma mulimbikepo ndi kusadya mwaziwo; popeza mwazi ndiwo moyo, nimusamadya moyo pamodzi ndi nyama yake.


Mwazi wake wokha musamadya; muuthire pansi ngati madzi.


Pakuti cholengedwa chonse cha Mulungu nchabwino, ndipo palibe kanthu kayenera kutayika, ngati kalandiridwa ndi chiyamiko;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa