Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Levitiko 11:1 - Buku Lopatulika

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati nao,

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati nao,

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Chauta adauza Mose ndi Aroni kuti,

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Yehova anayankhula ndi Mose ndi Aaroni kuti,

Onani mutuwo Koperani




Levitiko 11:1
10 Mawu Ofanana  

Nyama zonse zodyedwa udzitengereko wekha zisanu ndi ziwiri, zisanu ndi ziwiri, yamphongo ndi yaikazi yake; ndi nyama zosadyedwa ziwiriziwiri yamphongo ndi yaikazi yake.


Ndipo Nowa anamanga guwa la nsembe la Yehova; natengapo nyama zodyedwa zonse ndi mbalame zodyedwa zonse napereka nsembe zopsereza paguwapo.


Zoyenda zonse zamoyo zidzakhala zakudya zanu; monga therere laliwisi ndakupatsani inu zonsezo.


Pamene Mose adamva ichi chidamkomera pamaso pake.


Nenani ndi ana a Israele, ndi kuti, Izi ndi zamoyo zimene muyenera kumadya mwa nyama zonse zili padziko lapansi.


Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati,


Potero musiyanitse pakati pa nyama zoyera ndi nyama zodetsa, ndi pakati pa mbalame zodetsa ndi zoyera; ndipo musadzinyansitsa ndi nyama, kapena mbalame, kapena ndi kanthu kalikonse kakukwawa pansi, kamene ndinakusiyanitsirani kakhale kodetsa.


Koma Petro anati, Iaitu, Mbuye; pakuti sindinadye ine ndi kale lonse kanthu wamba ndi konyansa.


Nyamazi muyenera kumadya ndi izi: ng'ombe, nkhosa, ndi mbuzi,


Musatengedwe ndi maphunzitso a mitundumitundu, ndi achilendo; pakuti nkokoma kuti mtima ukhazikike ndi chisomo; kosati ndi zakudya, zimene iwo adazitsata sanapindule nazo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa