Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Levitiko 10:13 - Buku Lopatulika

13 ndipo muziidyera kumalo kopatulika, popeza ndiyo gawo lako, ndi gawo la ana ako, lochokera ku nsembe zamoto za Yehova; pakuti anandiuza chotero.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

13 ndipo muziidyera kumalo kopatulika, popeza ndiyo gawo lako, ndi gawo la ana ako, lochokera ku nsembe zamoto za Yehova; pakuti anandiuza chotero.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

13 Muzidye pa malo oyera, chifukwa zimenezi ndakugaŵiraniko kuchokera pa nsembe yotentha pa moto yopereka kwa Chauta, kuti zikhale zanu, iwe ndi ana ako. Ndithudi, zimenezi ndizo zimene Chauta adandilamula.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

13 Muzidye pa malo wopatulika chifukwa zimenezi ndi gawo lako ndi la ana ako pa zopereka zopsereza kwa Yehova. Izitu ndi zimene Yehova anandilamulira.

Onani mutuwo Koperani




Levitiko 10:13
7 Mawu Ofanana  

Pamenepo anati kwa ine, Zipinda za kumpoto, ndi zipinda za kumwera, zili chakuno cha mpatawo, ndizo zipinda zopatulika, kumene ansembe okhala pafupi pa Yehova azidyera zinthu zopatulika kwambiri; kumeneko aziika zopatulika kwambiri, ndi nsembe yaufa, ndi nsembe yauchimo, ndi nsembe yopalamula; pakuti malowo ndi opatulika.


Ndipo Mose ananena ndi Aroni, ndi Eleazara ndi Itamara, ana ake otsala, Tengani nsembe yaufa yotsalira ku nsembe zamoto za Yehova, ndi kuidya yopanda chotupitsa pafupi paguwa la nsembe; pakuti ndiyo yopatulika kwambiri;


Ndi nganga yoweyula ndi mwendo wokweza mudyere izi pamalo poyera; iwe ndi ana ako aamuna, ndi ana ako aakazi omwe, popeza zapatsidwa gawo lako ndi gawo la ana ako aamuna, zochokera ku nsembe zoyamika za ana a Israele.


Ndipo chotsalira cha nsembe yaufa chikhale cha Aroni ndi ana ake; ndicho chopatulika kwambiri cha nsembe zamoto za Yehova.


Ndipo chotsalira chake adye Aroni ndi ana ake; achidye chopanda chotupitsa m'malo opatulika; pa bwalo la chihema chokomanako achidye.


Muzizidya izi monga zopatulika kwambiri; mwamuna yense adyeko; uziyese zopatulika.


Zopatulika za munthu aliyense ndi zake: zilizonse munthu aliyense akapatsa wansembe, zisanduka zake.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa