Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Genesis 34:20 - Buku Lopatulika

20 Ndipo Hamori ndi Sekemu mwana wake anafika ku chipata cha mzinda wao, nalankhulana ndi anthu a mzinda wao, kuti,

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

20 Ndipo Hamori ndi Sekemu mwana wake anafika ku chipata cha mudzi wao, nalankhulana ndi anthu a mudzi wao, kuti,

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

20 Tsono Hamori pamodzi ndi mwana wake Sekemu adakachita msonkhano ku chipata cha mzinda wao, nalankhula ndi anthu a m'mudzi mwao kuti,

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

20 Choncho Hamori ndi mwana wake Sekemu anapita ku chipata cha mzinda wawo kukayankhula ndi anthu a mu mzindawo.

Onani mutuwo Koperani




Genesis 34:20
14 Mawu Ofanana  

kudalitsa ndidzakudalitsa iwe, kuchulukitsa ndidzachulukitsa mbeu zako monga nyenyezi za kumwamba, monga mchenga wa m'mphepete mwa nyanja; ndipo mbeu zako zidzagonjetsa chipata cha adani ao;


Ndipo Efuroni anakhala pakati pa ana a Hiti, ndipo Efuroni Muhiti anayankha Abrahamu alinkumva ana a Hiti, onse amene analowa pa chipata cha mzinda wake, kuti,


Ndipo mnyamatayo sanachedwe kuchichita popeza anakondwera ndi mwana wake wamkazi wa Yakobo; ndipo iye anali wolemekezedwa woposa onse a pa banja la atate wake.


Anthu amenewa ali amtendere pamodzi ndi ife; chifukwa chake akhale m'dzikomo, achite malonda m'menemo: pakuti taonani dzikolo lili lalikulu lokwanira iwo; tidzitengere ana ao aakazi akhale aakazi athu, tiwapatse amenewa ana athu aakazi.


Ndipo Abisalomu analawirira, nakaima panjira ya kuchipata; ndipo kunatero, pakakhala munthu aliyense ndi mlandu woyenera kufika kwa mfumu kuti aweruze, Abisalomu anamuitana, nati, Ndinu wa kumzinda uti? Ndipo anati, Mnyamata wanu ndiye wa fuko lina la Aisraele.


Muja ndinatuluka kunka kuchipata kumzinda, muja ndinakonza pokhala panga kukhwalala,


Wodala munthu amene anadzaza nayo phodo lake: sadzachita manyazi iwo, pakulankhula nao adani kuchipata.


Mwamuna wake adziwika kubwalo, pokhala pakati pa akulu a dziko.


Iwo adana naye wodzudzula kuchipata, nanyansidwa naye wolunjikitsa mau.


Pakuti ndidziwa kuti zolakwa zanu nzochuluka, ndi machimo anu ndi olimba, inu akusautsa olungama, akulandira chokometsera mlandu, akukankha osowa kuchipata.


Danani nacho choipa, nimukonde chokoma; nimukhazikitse chiweruzo kuchipata; kapena Yehova Mulungu wa makamu adzachitira chifundo otsala a Yosefe.


Izi ndizo muzichite: Nenani choonadi yense ndi mnzake; weruzani zoona ndi chiweruzo cha mtendere m'zipata zanu;


pamenepo mutulutse mwamunayo kapena mkaziyo, anachita choipacho, kunka naye ku zipata zanu, ndiye wamwamuna kapena wamkazi; ndipo muwaponye miyala, kuti afe.


Ndipo Bowazi anakwera kunka kuchipata, nakhala pansi pomwepo; ndipo taona, woombolera winayo adanena Bowazi analinkupita; nati iye, Iwe uje, patuka, khala pansi apa; napatuka iye, nakhala pansi.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa